< Miyambo 17 >

1 Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
Melhor é um pedaço seco de comida com tranquilidade, do que uma casa cheia de carne com briga.
2 Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
O servo prudente dominará o filho causador de vergonha, e receberá parte da herança entre os irmãos.
3 Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
O crisol é para a prata, e o forno para o ouro; mas o SENHOR prova os corações.
4 Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
O malfeitor presta atenção ao lábio injusto; o mentiroso inclina os ouvidos à língua maligna.
5 Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
Quem ridiculariza o pobre insulta o seu Criador; aquele que se alegra da calamidade não ficará impune.
6 Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
A coroa dos idosos [são] os filhos de seus filhos; e a glória dos filhos são seus pais.
7 Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
Não é adequado ao tolo falar com elegância; muito menos para o príncipe falar mentiras.
8 Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
O presente é [como] uma pedra preciosa aos olhos de seus donos; para onde quer que se voltar, [tentará] ter algum proveito.
9 Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
Quem perdoa a transgressão busca a amizade; mas quem repete o assunto afasta amigos íntimos.
10 Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
A repreensão entra mais profundamente no prudente do que cem açoites no tolo.
11 Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
Na verdade quem é mal busca somente a rebeldia; mas o mensageiro cruel será enviado contra ele.
12 Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
[É melhor] ao homem encontrar uma ursa roubada [de seus filhotes], do que um tolo em sua loucura.
13 Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
Quanto ao que devolve o mal no lugar do bem, o mal nunca se afastará de sua casa.
14 Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
Começar uma briga é [como] deixar águas rolarem; por isso, abandona a discussão antes que haja irritação.
15 Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
Quem absolve ao perverso e quem condena ao justo, ambos são abomináveis ao SENHOR.
16 Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
Para que serve o dinheiro na mão do tolo, já que ele não tem interesse em obter sabedoria?
17 Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
O amigo ama em todo tempo, e o irmão nasce para [ajudar] na angústia.
18 Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
O homem imprudente assume compromisso, ficando como fiador de seu próximo.
19 Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
Quem ama a briga, ama a transgressão; quem constrói alta sua porta busca ruína.
20 Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
O perverso de coração nunca encontrará o bem; e quem distorce [as palavras de] sua língua cairá no mal.
21 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
Quem gera o louco [cria] sua própria tristeza; e o pai do imprudente não se alegrará.
22 Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
O coração alegre é um bom remédio, mas o espírito abatido faz os ossos se secarem.
23 Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
O perverso toma o presente do seio, para perverter os caminhos da justiça.
24 Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
A sabedoria está diante do rosto do prudente; porém os olhos do tolo [estão voltados] para os confins da terra.
25 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
O filho tolo é tristeza para seu pai, e amargura para aquela que o gerou.
26 Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
Também não é bom punir ao justo, nem bater nos príncipes por causa da justiça.
27 Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
Quem entende o conhecimento guarda suas palavras; [e] o homem de bom entendimento [é] de espírito calmo.
28 Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.
Até o tolo, quando está calado, é considerado como sábio; [e] quem fecha seus lábios, como de bom senso.

< Miyambo 17 >