< Miyambo 17 >

1 Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
لقمه خشک با سلامتی، بهتر است ازخانه پر از ضیافت با مخاصمت.۱
2 Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
بنده عاقل بر پسر پست فطرت مسلط خواهدبود، و میراث را با برادران تقسیم خواهد نمود.۲
3 Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
بوته برای نقره و کوره به جهت طلا است، اماخداوند امتحان کننده دلها است.۳
4 Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
شریر به لبهای دروغگو اصغا می‌کند، و مردکاذب به زبان فتنه انگیز گوش می‌دهد.۴
5 Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
هر‌که فقیر را استهزا کند آفریننده خویش رامذمت می‌کند، و هر‌که از بلا خوش می‌شودبی سزا نخواهد ماند.۵
6 Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
تاج پیران، پسران پسرانند، و جلال فرزندان، پدران ایشانند.۶
7 Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
کلام کبرآمیز احمق را نمی شاید، و چندمرتبه زیاده لبهای دروغگو نجبا را.۷
8 Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
هدیه در نظر اهل آن سنگ گرانبها است که هر کجا توجه نماید برخوردار می‌شود.۸
9 Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
هر‌که گناهی را مستور کند طالب محبت می‌باشد، اما هر‌که امری را تکرار کند دوستان خالص را از هم جدا می‌سازد.۹
10 Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
یک ملامت به مرد فهیم اثر می‌کند، بیشتراز صد تازیانه به مرد جاهل.۱۰
11 Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
مرد شریر طالب فتنه است و بس. لهذاقاصد ستمکیش نزد او فرستاده می‌شود.۱۱
12 Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
اگر خرسی که بچه هایش کشته شود به انسان برخورد، بهتر است از مرد احمق در حماقت خود.۱۲
13 Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
کسی‌که به عوض نیکویی بدی می‌کند بلااز خانه او دور نخواهد شد.۱۳
14 Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
ابتدای نزاع مثل رخنه کردن آب است، پس مخاصمه را ترک کن قبل از آنکه به مجادله برسد.۱۴
15 Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
هر‌که شریر را عادل شمارد و هر‌که عادل را ملزم سازد، هر دوی ایشان نزد خداوندمکروهند.۱۵
16 Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
قیمت به جهت خریدن حکمت چرا به‌دست احمق باشد؟ و حال آنکه هیچ فهم ندارد.۱۶
17 Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
دوست خالص در همه اوقات محبت می‌نماید، و برادر به جهت تنگی مولود شده است.۱۷
18 Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
مرد ناقص العقل دست می‌دهد و در حضورهمسایه خود ضامن می‌شود.۱۸
19 Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
هر‌که معصیت را دوست دارد منازعه رادوست می‌دارد، و هر‌که در خود را بلند سازدخرابی را می‌طلبد.۱۹
20 Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
کسی‌که دل کج دارد نیکویی را نخواهدیافت. و هر‌که زبان دروغگو دارد در بلا گرفتارخواهد شد.۲۰
21 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
هر‌که فرزند احمق آورد برای خویشتن غم پیدا می‌کند، و پدر فرزند ابله شادی نخواهد دید.۲۱
22 Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
دل‌شادمان شفای نیکو می‌بخشد، اما روح شکسته استخوانها را خشک می‌کند.۲۲
23 Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
مرد شریر رشوه را از بغل می‌گیرد، تاراههای انصاف را منحرف سازد.۲۳
24 Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
حکمت در مد نظر مرد فهیم است، اماچشمان احمق در اقصای زمین می‌باشد.۲۴
25 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
پسر احمق برای پدر خویش حزن است، وبه جهت مادر خویش تلخی است.۲۵
26 Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
عادلان را نیز سرزنش نمودن خوب نیست، و نه ضرب زدن به نجبا به‌سبب راستی ایشان.۲۶
27 Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
صاحب معرفت سخنان خود را بازمی دارد، و هر‌که روح حلیم دارد مرد فطانت پیشه است.۲۷
28 Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.
مرد احمق نیز چون خاموش باشد او راحکیم می‌شمارند، و هر‌که لبهای خود را می‌بنددفهیم است.۲۸

< Miyambo 17 >