< Miyambo 17 >

1 Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
Bedre et stykke tørt brød med ro og fred enn et hus fullt av slakt med trette.
2 Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
En klok tjener får råde over en dårlig sønn, og iblandt brødrene får han del i arven.
3 Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
Der er digel for sølv og ovn for gull; men den som prøver hjertene, er Herren.
4 Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
Den onde akter på ondskaps lebe; løgneren lytter til ødeleggelses tunge.
5 Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
Den som spotter den fattige, håner hans skaper; den som gleder sig over ulykke, skal ikke bli ustraffet.
6 Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
De gamles krone er barnebarn, og barns pryd er deres fedre.
7 Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
Det sømmer sig ikke for dåren å tale store ord, enn mindre for den høibårne å tale løgn.
8 Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
Gave er en edelsten i dens øine som får den; hvor den kommer, gjør den lykke.
9 Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
Den som dekker over overtredelse, søker kjærlighet; men den som ripper op en sak, skiller venn fra venn.
10 Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
Skjenn virker bedre på den forstandige enn hundre slag på dåren.
11 Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
En ond manns hu står bare til gjenstridighet, og en ubarmhjertig engel sendes imot ham.
12 Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
Bedre for en mann å møte en bjørn som ungene er tatt fra, enn en dåre i hans dårskap.
13 Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
Den som gjengjelder godt med ondt, fra hans hus skal ulykken ikke vike.
14 Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
Å begynne trette er som å åpne for vann; la da tretten fare, før den blir for voldsom!
15 Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
Den som frikjenner en ugudelig, og den som domfeller en rettferdig, de er begge to en vederstyggelighet for Herren.
16 Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
Hvad hjelper penger i dårens hånd til å kjøpe visdom, siden han er uten forstand?
17 Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
En venn elsker alltid, og en bror fødes til hjelp i nød.
18 Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
Et menneske som ikke har forstand, gir håndslag og går i borgen hos sin næste.
19 Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
Den som elsker trette, elsker synd; den som gjør sin dør høi, søker sin egen undergang.
20 Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
Den som er falsk i hjertet, finner intet godt, og den som er vrang i sin tale, faller i ulykke.
21 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
Den som har en narr til sønn, får sorg av ham; en dåres far har ingen glede.
22 Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
Et glad hjerte gir god lægedom, men et nedslått mot tar margen fra benene.
23 Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
Den ugudelige tar gaver ut av barmen for å bøie rettens gang.
24 Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
Den forstandige har visdommen for øie, men dårens øine er ved jordens ende.
25 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
En uforstandig sønn er en gremmelse for sin far og en bitter sorg for henne som fødte ham.
26 Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
Å straffe også den rettferdige er ikke godt; å slå edle menn er tvert imot all rett.
27 Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
Den som er sparsom med sine ord, er klok, og den koldsindige er en forstandig mann.
28 Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.
Også dåren aktes for klok når han tier, for vis når han holder sine leber lukket.

< Miyambo 17 >