< Miyambo 17 >

1 Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
Better is a dry morsel, and quietness therewith, than a house full of feasting [with] strife.
2 Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
A wise servant shall rule over a son that causeth shame, and shall have part in the inheritance among the brethren.
3 Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
The fining-pot is for silver, and the furnace for gold; but Jehovah trieth the hearts.
4 Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
The evil-doer giveth heed to iniquitous lips; the liar giveth ear to a mischievous tongue.
5 Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
Whoso mocketh a poor [man] reproacheth his Maker; he that is glad at calamity shall not be held innocent.
6 Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
Children's children are the crown of old men; and the glory of children are their fathers.
7 Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
Excellent speech becometh not a vile [man]; how much less do lying lips a noble!
8 Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
A gift is a precious stone in the eyes of the possessor: whithersoever it turneth it prospereth.
9 Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
He that covereth transgression seeketh love; but he that bringeth a matter up again separateth very friends.
10 Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
A reproof entereth more deeply into him that hath understanding than a hundred stripes into a fool.
11 Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
An evil [man] seeketh only rebellion; but a cruel messenger shall be sent against him.
12 Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
Let a bear robbed of her whelps meet a man rather than a fool in his folly.
13 Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
Whoso rewardeth evil for good, evil shall not depart from his house.
14 Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
The beginning of contention is [as] when one letteth out water; therefore leave off strife before it become vehement.
15 Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
He that justifieth the wicked, and he that condemneth the righteous, even they both are abomination to Jehovah.
16 Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
To what purpose is there a price in the hand of a fool to get wisdom, seeing [he] hath no sense?
17 Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
The friend loveth at all times, and a brother is born for adversity.
18 Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
A senseless man striketh hands, becoming surety for his neighbour.
19 Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
He loveth transgression that loveth a quarrel; he that maketh high his gate seeketh destruction.
20 Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
He that hath a perverse heart findeth no good; and he that shifteth about with his tongue falleth into evil.
21 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
He that begetteth a fool [doeth it] to his sorrow, and the father of a vile [man] hath no joy.
22 Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
A joyful heart promoteth healing; but a broken spirit drieth up the bones.
23 Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
A wicked [man] taketh a gift out of the bosom, to pervert the paths of judgment.
24 Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
Wisdom is before him that hath understanding; but the eyes of a fool are in the ends of the earth.
25 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
A foolish son is a grief to his father, and bitterness to her that bore him.
26 Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
To punish a righteous [man] is not good, nor to strike nobles because of [their] uprightness.
27 Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
He that hath knowledge spareth his words; and a man of understanding is of a cool spirit.
28 Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.
Even a fool when he holdeth his peace is reckoned wise, [and] he that shutteth his lips, intelligent.

< Miyambo 17 >