< Miyambo 17 >

1 Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
A dry morsel with gladness is better than a house full of sacrifices along with conflict.
2 Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
A wise servant shall rule over foolish sons, and he will divide the inheritance among brothers.
3 Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
Just as silver is tested by fire, and gold is tested in the furnace, so also does the Lord test hearts.
4 Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
The evil obey an unjust tongue. And the false are submissive to lying lips.
5 Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
Whoever despises the poor rebukes his Maker. And whoever rejoices in the ruin of another will not go unpunished.
6 Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
Sons of sons are the crown of old age. And the glory of sons is their fathers.
7 Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
Well-chosen words are not fitting for the foolish, nor are lying lips fitting for a leader.
8 Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
The expectation of those who stand ready is a most pleasing jewel. Whichever way he turns himself, he understands prudently.
9 Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
Whoever conceals an offense seeks friendships. Whoever repeats the words of another separates allies.
10 Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
A correction benefits more with a wise man, than a hundred stripes with a fool.
11 Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
The evil one continually seeks conflicts. But a cruel Angel shall be sent against him.
12 Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
It is more expedient to meet a bear robbed of her young, than the foolish trusting in his own folly.
13 Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
Whoever repays evil for good, evil shall not withdraw from his house.
14 Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
Whoever releases the water is the head of the conflict. And just before he suffers contempt, he abandons judgment.
15 Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
Those who justify the impious, and those who condemn the just, both are abominable with God.
16 Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
What does it profit the foolish to have riches, when he is not able to buy wisdom? Whoever makes his house high seeks ruin. And whoever shuns learning shall fall into evils.
17 Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
Whoever is a friend loves at all times. And a brother is proved by distress.
18 Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
A foolish man will clap his hands, when he makes a pledge for his friend.
19 Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
Whoever dwells on discord loves disputes. And whoever exalts his door seeks ruin.
20 Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
Whoever is of a perverse heart shall not find good. And whoever turns his tongue shall fall into evil.
21 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
A foolish one is born into his own disgrace. But his father will not rejoice in one who is senseless.
22 Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
A joyful soul makes a lifetime flourish. A gloomy spirit dries out the bones.
23 Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
The impious receives gifts from the bosom, so that he may pervert the paths of judgment.
24 Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
Prudence shines from the face of the wise. The eyes of the foolish are on the ends of the earth.
25 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
A foolish son is the anger of the father and the grief of the mother who conceived him.
26 Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
It is not good to inflict damage on the just, nor to strike the leader who judges uprightly.
27 Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
Whoever moderates his words is learned and prudent. And a man of learning has a precious spirit.
28 Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.
If he would remain silent, even the foolish would be considered wise, and if he closes his lips, intelligent.

< Miyambo 17 >