< Miyambo 17 >

1 Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
Better a dry morsel in quietness than a house full of feasting with strife.
2 Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
A wise servant will rule over a disgraceful son and share his inheritance as one of the brothers.
3 Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
A crucible for silver and a furnace for gold, but the LORD is the tester of hearts.
4 Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
A wicked man listens to evil lips; a liar gives ear to a destructive tongue.
5 Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
He who mocks the poor insults their Maker; whoever gloats over calamity will not go unpunished.
6 Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
Grandchildren are the crown of the aged, and the glory of a son is his father.
7 Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
Eloquent words are unfit for a fool; how much worse are lying lips to a ruler!
8 Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
A bribe is a charm to its giver; wherever he turns, he succeeds.
9 Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
Whoever conceals an offense promotes love, but he who brings it up separates friends.
10 Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
A rebuke cuts into a man of discernment deeper than a hundred lashes cut into a fool.
11 Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
An evil man seeks only rebellion; a cruel messenger will be sent against him.
12 Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
It is better to meet a bear robbed of her cubs than a fool in his folly.
13 Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
If anyone returns evil for good, evil will never leave his house.
14 Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
To start a quarrel is to release a flood; so abandon the dispute before it breaks out.
15 Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
Acquitting the guilty and condemning the righteous— both are detestable to the LORD.
16 Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
Why should the fool have money in his hand with no intention of buying wisdom?
17 Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
A friend loves at all times, and a brother is born for adversity.
18 Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
A man lacking judgment strikes hands in pledge and puts up security for his neighbor.
19 Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
He who loves transgression loves strife; he who builds his gate high invites destruction.
20 Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
The one with a perverse heart finds no good, and he whose tongue is deceitful falls into trouble.
21 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
A man fathers a fool to his own grief; the father of a fool has no joy.
22 Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
A joyful heart is good medicine, but a broken spirit dries up the bones.
23 Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
A wicked man takes a covert bribe to subvert the course of justice.
24 Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
Wisdom is the focus of the discerning, but the eyes of a fool wander to the ends of the earth.
25 Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
A foolish son brings grief to his father and bitterness to her who bore him.
26 Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
It is surely not good to punish the innocent or to flog a noble for his honesty.
27 Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
A man of knowledge restrains his words, and a man of understanding maintains a calm spirit.
28 Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.
Even a fool is considered wise if he keeps silent, and discerning when he holds his tongue.

< Miyambo 17 >