< Miyambo 16 >
1 Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
İnsan aklıyla çok şey tasarlayabilir, Ama dilin vereceği yanıt RAB'dendir.
2 Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
İnsan her yaptığını temiz sanır, Ama niyetlerini tartan RAB'dir.
3 Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
Yapacağın işleri RAB'be emanet et, O zaman tasarıların gerçekleşir.
4 Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
RAB her şeyi amacına uygun yapar, Kötü kişinin yıkım gününü de O hazırlar.
5 Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
RAB yüreği küstah olandan iğrenir, Bilin ki, öyleleri cezasız kalmaz.
6 Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
Sevgi ve bağlılık suçları bağışlatır, RAB korkusu insanı kötülükten uzaklaştırır.
7 Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
RAB kişinin yaşayışından hoşnutsa Düşmanlarını bile onunla barıştırır.
8 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
Doğrulukla kazanılan az şey Haksızlıkla kazanılan büyük gelirden iyidir.
9 Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
Kişi yüreğinde gideceği yolu tasarlar, Ama adımlarını RAB yönlendirir.
10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
Tanrı buyruklarını kralın ağzıyla açıklar, Bu nedenle kral adaleti çiğnememelidir.
11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
Doğru terazi ve baskül RAB'bindir, Bütün tartı ağırlıklarını O belirler.
12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
Krallar kötülükten iğrenir, Çünkü tahtın güvencesi adalettir.
13 Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
Kral doğru söyleyenden hoşnut kalır, Dürüst konuşanı sever.
14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
Kralın öfkesi ölüm habercisidir, Ama bilge kişi onu yatıştırır.
15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
Kralın yüzü gülüyorsa, yaşam demektir. Lütfu son yağmuru getiren bulut gibidir.
16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
Bilgelik kazanmak altından daha değerlidir, Akla sahip olmak da gümüşe yeğlenir.
17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
Dürüstlerin tuttuğu yol kötülükten uzaklaştırır, Yoluna dikkat eden, canını korur.
18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
Gururun ardından yıkım, Kibirli ruhun ardından da düşüş gelir.
19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
Mazlumlar arasında alçakgönüllü biri olmak, Kibirlilerle çapul malı paylaşmaktan iyidir.
20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
Öğüde kulak veren başarıya ulaşır, RAB'be güvenen mutlu olur.
21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
Bilge yüreklilere akıllı denir, Tatlı söz ikna gücünü artırır.
22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
Sağduyu, sahibine yaşam kaynağı, Ahmaklıksa ahmaklara cezadır.
23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
Bilgenin aklı diline yön verir, Dudaklarının ikna gücünü artırır.
24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
Hoş sözler petek balı gibidir, Cana tatlı ve bedene şifadır.
25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
Öyle yol var ki, insana düz gibi görünür, Ama sonu ölümdür.
26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
Emekçinin iştahıdır onu çalıştıran, Çünkü açlığı onu kamçılar.
27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
Alçaklar başkalarına kötülük tasarlar, Konuşmaları kavurucu ateş gibidir.
28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
Huysuz kişi çekişmeyi körükler, Dedikoducu can dostları ayırır.
29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
Zorba kişi başkalarını ayartır Ve onları olumsuz yola yöneltir.
30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
Göz kırpmak düzenbazlığa, Sinsi gülücükler kötülüğe işarettir.
31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
Ağarmış saçlar onur tacıdır, Doğru yaşayışla kazanılır.
32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
Sabırlı kişi yiğitten üstündür, Kendini denetleyen de kentler fethedenden üstündür.
33 Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.
İnsan kura atar, Ama her kararı RAB verir.