< Miyambo 16 >

1 Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
En menniska sätter sig väl före i hjertat; men af Herranom kommer, hvad tungan tala skall.
2 Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
Hvarjom och enom tyckas hans vägar rene vara; men Herren allena gör hjertat visst.
3 Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
Befalla Herranom din verk, så gå din anslag fram.
4 Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
Herren gör all ting för sin egen skull; desslikes ock den ogudaktiga till en ondan dag.
5 Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
All högmodig hjerta äro Herranom en styggelse, och skola icke ostraffad blifva, om de än alle tillhopa höllo.
6 Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
Genom godhet och trohet varder en missgerning försonad, och genom Herrans fruktan undflyr man det onda.
7 Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
Om någors mans vägar behaga Herranom, så gör han ock hans ovänner tillfrids med honom.
8 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
Bättre är litet med rättfärdighet, än mycken tilldrägt med orätt.
9 Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
Menniskones hjerta sätter sig sina vägar före; men Herren allena gifver, att de framgår.
10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
Prophetia ( är ) i Konungens mun; hans mun felar intet i domen.
11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
Rätt våg och vigt är af Herranom; och all pund i säckenom äro hans verk.
12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
Om Konungarna orätt göra, så äro de en styggelse; ty genom rättfärdighet varder Konungssätet fast.
13 Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
Rätt råd behagar Konungenom, och den som rätt råder, han varder älskad.
14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
Konungens vrede är dödsens bådskap, och en vis man försonar honom.
15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
När Konungens ansigte är ljufligit, det är lifvet, och hans ynnest är såsom ett aftonregn.
16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
Tag vishet till dig, ty hon är bättre än guld; och hafva förstånd är ädlare än silfver.
17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
De frommas väg flyr det arga, och den sin väg bevarar, han behåller sitt lif.
18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
Den som ett nederfall skall få, han varder tillförene högmodig, och stort sinne går för fallet.
19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
Bättre är ödmjuk vara med de elända, än utskifta rof med de högfärdiga.
20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
Den ena sak visliga företager, han finner lycko, och säll är den som sig förlåter på Herran.
21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
En förståndig varder berömd for en vis man, och ljuft tal lärer väl.
22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
Klokhet är en lefvandes källa honom, som hafver henne; men de dårars tuktan är galenskap.
23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
Ett vist hjerta talar klokliga, och lärer väl.
24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
Ljuftig ord äro en hannogskaka; de trösta själena, och uppfriska benen.
25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
Mångom behagar en väg väl, men hans yttersta drager till döden.
26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
Mången man kommer i stor olycko genom sin egen mun.
27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
En lösaktig menniska gräfver efter olycko, och i hennes mun brinner eld.
28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
En vrång menniska kommer träto åstad, och en lackare gör Förstar oens.
29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
En arg menniska lockar sin nästa, och förer honom in på en ondan väg.
30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
Den som blinkar med ögonen, han tänker intet godt; och den som biter läpparna, han fullkomnar ondt.
31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
Gå hår äro en hederskrona, den på rättfärdighetenes väg funnen varder.
32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
En tålig man är bättre än en stark; och den, som råder sitt sinne, är bättre än en som städer vinner.
33 Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.
Lotten varder kastad i skötet; men han faller hvart Herren vill.

< Miyambo 16 >