< Miyambo 16 >
1 Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
Do homem são as preparações do coração, mas do Senhor a resposta da boca.
2 Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
Todos os caminhos do homem são limpos aos seus olhos, mas o Senhor pesa os espíritos.
3 Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
Confia do Senhor as tuas obras, e teus pensamentos serão estabelecidos.
4 Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
O Senhor fez todas as coisas para si, para os seus próprios fins, e até ao ímpio para o dia do mal.
5 Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
Abominação é ao Senhor todo o altivo de coração: ainda que ele junte mão à mão, não será inocente
6 Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
Pela misericórdia e pela fidelidade se expia a iniquidade, e pelo temor do Senhor os homens se desviam do mal.
7 Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
Sendo os caminhos do homem agradáveis ao Senhor, até a seus inimigos faz que tenham paz com ele.
8 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
Melhor é o pouco com justiça, do que a abundância de colheita com injustiça.
9 Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
O coração do homem considera o seu caminho, mas o Senhor lhe dirige os passos.
10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
Adivinhação se acha nos lábios do rei: em juízo não prevaricará a sua boca.
11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
O peso e a balança justa são do Senhor: obra sua são todos os pesos da bolsa.
12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
Abominação é para os reis obrarem impiedade, porque com justiça se estabelece o trono.
13 Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
Os lábios de justiça são o contentamento dos reis, e eles amarão ao que fala coisas retas.
14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
O furor do rei é como uns mensageiros da morte, mas o homem sábio o apaziguará.
15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
Na luz do rosto do rei está a vida, e a sua benevolência é como a nuvem da chuva serodia.
16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
Quanto melhor é adquirir a sabedoria do que o ouro! e quanto mais excelente adquirir a prudência do que a prata!
17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
A carreira dos retos é desviar-se do mal; o que guarda a sua alma conserva o seu caminho.
18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
A soberba precede a ruína, e a altivez do espírito precede a queda.
19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
Melhor é ser humilde de espírito com os mansos, do que repartir o despojo com os soberbos.
20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
O que atenta prudentemente para a palavra achará o bem, e o que confia no Senhor será bem-aventurado.
21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
O sábio de coração será chamado prudente, e a doçura dos lábios aumentará o ensino.
22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
O entendimento, para aqueles que o possuem, é uma fonte de vida, mas a instrução dos tolos é a sua estultícia.
23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
O coração do sábio instrui a sua boca, e sobre os seus lábios aumentará a doutrina.
24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
Favo de mel são as palavras suaves, doces para a alma, e saúde para os ossos.
25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
Há caminho, que parece direito ao homem, mas o seu fim são os caminhos da morte.
26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
O trabalhador trabalha para si mesmo, porque a sua boca o insta.
27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
O homem de Belial cava o mal, e nos seus lábios se acha como um fogo ardente.
28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
O homem perverso levanta a contenda, e o murmurador separa os maiores amigos.
29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
O homem violento persuade ao seu companheiro, e o guia por caminho não bom.
30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
Fecha os olhos para imaginar perversidades; mordendo os lábios, efetua o mal.
31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
Coroa de honra são as cãs, achando-se elas no caminho de justiça.
32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
Melhor é o longânimo do que o valente, e o que governa o seu espírito do que o que toma uma cidade.
33 Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.
A sorte se lança no regaço, mas do Senhor procede toda a sua disposição.