< Miyambo 16 >
1 Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
Człowiek sporządza myśli serca swego; ale od Pana jest odpowiedź języka.
2 Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
Wszystkie drogi człowiecze zdadzą się być czyste przed oczyma jego; ale Pan jest, który waży serca.
3 Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
Włóż na Pana sprawy twe, a będą utwierdzone zamysły twoje.
4 Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
Pan dla siebie samego wszystko sprawił, nawet i niezbożnika na dzień zły.
5 Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
Obrzydliwością jest Panu każdy wyniosłego serca; który choć sobie innych na pomoc weźmie, nie ujdzie pomsty.
6 Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
Miłosierdziem i prawdą oczyszczona bywa nieprawość, a w bojaźni Pańskiej odstępujemy od złego.
7 Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
Gdy się podobają Panu drogi człowieka, i nieprzyjaciół jego do zgody z nim przywodzi.
8 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
Lepsza jest trocha z sprawiedliwością, niż wiele dochodów niesprawiedliwych.
9 Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
Serce człowiecze rozrządza drogi swe; ale Pan sprawuje kroki jego.
10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
Sprawiedliwy rozsądek jest w wargach królewskich; w sądzie nie błądzą usta jego.
11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
Waga i szale są ustawą Pańską, a wszystkie gwichty sprawiedliwe w worku są za sprawą jego.
12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
Obrzydliwością jest królom czynić niezbożność; bo sprawiedliwością stolica umocniona bywa.
13 Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
Przyjemne są królom wargi sprawiedliwe, a szczerych w mowie miłują.
14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
Gniew królewski jest posłem śmierci; ale mąż mądry ubłaga go.
15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
W jasności twarzy królewskiej jest żywot, a łaska jego jest jako obłok z deszczem późnym.
16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
Daleko lepiej jest nabyć mądrości, niżeli złota najczystszego; a nabyć roztropności lepiej, niż srebra.
17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
Gościniec uprzejmych jest odstąpić od złego; strzeże duszy swej, kto strzeże drogi swojej.
18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
Przed zginieniem przychodzi pycha, a przed upadkiem wyniosłość ducha.
19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
Lepiej jest być uniżonego ducha z pokornymi, niżeli dzielić korzyści z pysznymi.
20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
Kto ma wzgląd na słowa, znajduje dobre; a kto ufa w Panu, błogosławiony jest.
21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
Kto jest mądrego serca, słynie rozumnym, a słodkość warg przydaje nauki.
22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
Zdrój żywota jest roztropność tym, którzy ją mają; ale umiejętność głupich jest głupstwem.
23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
Serce mądrego roztropnie sprawuje usta swoje, a wargami swemi przydaje nauki.
24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
Powieści wdzięczne są jako plastr miodu, słodkością duszy, a lekarstwem kościom.
25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
Zda się podczas droga być prosta człowiekowi; wszakże dokończenie jej pewna droga na śmierć.
26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
Człowiek pracowity pracuje sobie; bo go pobudzają usta jego.
27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
Człowiek niezbożny wykopuje złe, a w wargach jego jako ogień pałający.
28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
Mąż przewrotny rozsiewa zwady, a klatecznik rozłącza przyjaciół.
29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
Mąż okrutny przewabia bliźniego swego, i wprowadza go na drogę niedobrą.
30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
Kto mruga oczyma swemi, zmyśla przewrotności; a kto rucha wargami swemi, broi złe.
31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
Koroną chwały jest sędziwość; znajduje się na drodze sprawiedliwości.
32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
Lepszy jest nierychły do gniewu, niżeli mocarz; a kto panuje sercu swemu, lepszy jest, niżeli ten, co dobył miasta.
33 Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.
Los na łono rzucają; ale od Pana jest wszystko rozrządzenie jego.