< Miyambo 16 >

1 Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
לאדם מערכי לב ומיהוה מענה לשון׃
2 Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
כל דרכי איש זך בעיניו ותכן רוחות יהוה׃
3 Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
גל אל יהוה מעשיך ויכנו מחשבתיך׃
4 Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
כל פעל יהוה למענהו וגם רשע ליום רעה׃
5 Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
תועבת יהוה כל גבה לב יד ליד לא ינקה׃
6 Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
בחסד ואמת יכפר עון וביראת יהוה סור מרע׃
7 Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
ברצות יהוה דרכי איש גם אויביו ישלם אתו׃
8 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
טוב מעט בצדקה מרב תבואות בלא משפט׃
9 Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
לב אדם יחשב דרכו ויהוה יכין צעדו׃
10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
קסם על שפתי מלך במשפט לא ימעל פיו׃
11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
פלס ומאזני משפט ליהוה מעשהו כל אבני כיס׃
12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
תועבת מלכים עשות רשע כי בצדקה יכון כסא׃
13 Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
רצון מלכים שפתי צדק ודבר ישרים יאהב׃
14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
חמת מלך מלאכי מות ואיש חכם יכפרנה׃
15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
באור פני מלך חיים ורצונו כעב מלקוש׃
16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
קנה חכמה מה טוב מחרוץ וקנות בינה נבחר מכסף׃
17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
מסלת ישרים סור מרע שמר נפשו נצר דרכו׃
18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
לפני שבר גאון ולפני כשלון גבה רוח׃
19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
טוב שפל רוח את עניים מחלק שלל את גאים׃
20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
משכיל על דבר ימצא טוב ובוטח ביהוה אשריו׃
21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
לחכם לב יקרא נבון ומתק שפתים יסיף לקח׃
22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
מקור חיים שכל בעליו ומוסר אולים אולת׃
23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
לב חכם ישכיל פיהו ועל שפתיו יסיף לקח׃
24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
צוף דבש אמרי נעם מתוק לנפש ומרפא לעצם׃
25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
יש דרך ישר לפני איש ואחריתה דרכי מות׃
26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
נפש עמל עמלה לו כי אכף עליו פיהו׃
27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
איש בליעל כרה רעה ועל שפתיו כאש צרבת׃
28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
איש תהפכות ישלח מדון ונרגן מפריד אלוף׃
29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
איש חמס יפתה רעהו והוליכו בדרך לא טוב׃
30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
עצה עיניו לחשב תהפכות קרץ שפתיו כלה רעה׃
31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
עטרת תפארת שיבה בדרך צדקה תמצא׃
32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
טוב ארך אפים מגבור ומשל ברוחו מלכד עיר׃
33 Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.
בחיק יוטל את הגורל ומיהוה כל משפטו׃

< Miyambo 16 >