< Miyambo 16 >
1 Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
Čovjek snuje u srcu, a od Jahve je što će jezik odgovoriti.
2 Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
Čovjeku se svi njegovi putovi čine čisti, a Jahve ispituje duhove.
3 Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
Prepusti Jahvi svoja djela, i tvoje će se namisli ostvariti.
4 Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
Jahve je sve stvorio u svoju svrhu, pa i opakoga za dan zli.
5 Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
Mrzak je Jahvi svatko ohola duha: takav zaista ne ostaje bez kazne.
6 Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
Ljubavlju se i vjernošću pomiruje krivnja, i strahom se Gospodnjim uklanja zlo.
7 Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
Kad su Jahvi mili putovi čovječji, i neprijatelje njegove miri s njim.
8 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
Bolje je malo s pravednošću nego veliki dohoci s nepravdom.
9 Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
Srce čovječje smišlja svoj put, ali Jahve upravlja korake njegove.
10 Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
Proročanstvo je na usnama kraljevim: u osudi se njegova usta neće ogriješiti.
11 Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
Mjere i tezulje pripadaju Jahvi; njegovo su djelo i svi utezi.
12 Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
Mrsko je kraljevima počiniti opačinu, jer se pravdom utvrđuje prijestolje.
13 Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
Mile su kraljevima usne pravedne i oni ljube onog koji govori pravo.
14 Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
Jarost je kraljeva vjesnik smrti ali je mudar čovjek ublaži.
15 Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
U kraljevu je vedru licu život, i njegova je milost kao oblak s kišom proljetnom.
16 Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
Probitačnije je steći mudrost nego zlato, i stjecati razbor dragocjenije je nego srebro.
17 Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
Životni je put pravednih: kloniti se zla, i tko pazi na svoj put, čuva život svoj.
18 Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
Pred slomom ide oholost i pred padom uznositost.
19 Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
Bolje je biti krotak s poniznima nego dijeliti plijen s oholima.
20 Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
Tko pazi na riječ, nalazi sreću, i tko se uzda u Jahvu, blago njemu.
21 A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
Mudar srcem naziva se razumnim i prijazne usne uvećavaju znanje.
22 Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
Izvor je životni razum onima koji ga imaju, a ludima je kazna njihova ludost.
23 Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
Mudračev duh urazumljuje usta njegova, na usnama mu znanje umnožava.
24 Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
Saće meda riječi su ljupke, slatke duši i lijek kostima.
25 Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
Neki se put čini čovjeku prav, a na kraju vodi k smrti.
26 Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
Radnikova glad radi za nj; jer ga tjeraju usta njegova.
27 Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
Bezočnik pripravlja samo zlo i na usnama mu je oganj plameni.
28 Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
Himben čovjek zameće svađu i klevetnik razdor među prijatelje.
29 Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
Nasilnik zavodi bližnjega svoga i navodi ga na rđav put.
30 Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
Tko očima namiguje, himbu smišlja, a tko usne stišće, već je smislio pakost.
31 Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
Sijede su kose prekrasna kruna, nalaze se na putu pravednosti.
32 Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
Tko se teško srdi, bolji je od junaka, i tko nad sobom vlada, bolji je od osvojitelja grada.
33 Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.
U krilo plašta baca se kocka, ali je od Jahve svaka odluka.