< Miyambo 15 >

1 Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
Mulayim jawab ghezepni basar; Qopal söz achchiqni qozghar.
2 Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
Aqilanilerning tili bilimni jari qilar; Exmeqning aghzi quruq gep töker.
3 Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
Perwerdigarning közi her yerde yürer; Yaxshi-yamanlarni körüp turar.
4 Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
Shipa yetküzgüchi til xuddi bir «hayatliq derixi»dur; Tili egrilik kishining rohini sundurar.
5 Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
Exmeq atisining terbiyisige pisent qilmas; Lékin atisining tenbihige qulaq salghan zérek bolar.
6 Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
Heqqaniyning öyide göherler köptur; Biraq yamanning tapawiti özige awarichilik tapar.
7 Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
Dananing lewliri bilim tarqitar; Exmeqning könglidin héch bilim chiqmas.
8 Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
Yamanlarning qurbanliqi Perwerdigargha yirginchliktur; Duruslarning duasi Uning xursenlikidur.
9 Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
Yamanlarning yoli Perwerdigargha yirginchliktur; Lékin heqqaniyetni intilip izdigüchini U yaxshi körer.
10 Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
Toghra yoldin chiqqanlar azabliq terbiyini körer; Tenbihge öch bolghuchi öler.
11 Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol h7585)
Tehtisara we halaket Perwerdigarning köz aldida ochuq turghan yerde, Insan könglidiki oy-pikirni qandaqmu Uningdin yoshuralisun?! (Sheol h7585)
12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
Hakawur tenbih bergüchini yaqturmas; U aqilanilerdin nesihet élishqa barmas.
13 Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
Köngül shad bolsa, xush chiray bolar; Derd-elem tartsa, rohi sunar.
14 Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
Yorutulghan köngül bilimni izder; Eqilsizning aghzi nadanliqni ozuq qilar.
15 Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
Ézilgenlerning hemme künliri teste öter; Biraq shad köngül herkünini héyttek ötküzer.
16 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
Zor bayliq bilen biaramliq tapqandin, Azgha shükür qilip, Perwerdigardin eymen’gen ewzel.
17 Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
Nepret ichide yégen bordaq göshte qilin’ghan katta ziyapettin, Méhir-muhebbet ichide yégen köktat ewzel.
18 Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
Térikkek kishi jédel chiqirar; Éghir-bésiq talash-tartishlarni tinchlandurar.
19 Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
Hurunning yoli tikenlik qashadur, Durus ademning yoli kötürülgen yoldek daghdamdur.
20 Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
Dana oghul atisini shad qilar; Eqilsiz adem anisini kemsiter.
21 Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
Eqli yoq kishi exmeqliqi bilen xushtur; Yorutulghan kishi yolini toghrilap mangar.
22 Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
Meslihetsiz ish qilghanda nishanlar emelge ashmas; Meslihetchi köp bolghanda muddialar emelge ashurular.
23 Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
Kishige jayida bergen jawabidin xush bolar, Del waqtida qilghan söz neqeder yaxshidur!
24 Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol h7585)
Hayatliq yoli eqilliq kishini yuqirigha bashlayduki, Uni chongqur tehtisaradin qutquzar. (Sheol h7585)
25 Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
Perwerdigar tekebburning öyini yuluwéter; Biraq U tul xotunlargha pasillarni turghuzar.
26 Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
Yamanlarning oy-pikri Perwerdigargha yirginchliktur; Biraq sap dilning sözliri söyümlüktur.
27 Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
Ach köz kishi öz ailisige awarichilik keltürer; Para élishqa nepretlen’gen kishi kün körer.
28 Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
Heqqaniy adem qandaq jawab bérishte qayta-qayta oylinar; Yaman ademning aghzidin shumluq töküler.
29 Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
Perwerdigar yaman ademdin yiraqtur; Biraq U heqqaniyning duasini anglar.
30 Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
Xush közler köngülni shadlandurar; Xush xewer ustixanlargha gösh-may qondurar.
31 Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
Hayatliqqa élip baridighan tenbihke qulaq salghan kishi danalarning qataridin orun alar.
32 Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
Terbiyeni ret qilghan öz jénini xar qilar; Tenbihge qulaq salghan yorutular.
33 Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.
Perwerdigardin qorqush ademge danaliq ögiter; Awwal kemterlik bolsa, andin shöhret kéler.

< Miyambo 15 >