< Miyambo 15 >

1 Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
Jawabu la upole hugeuza ghadhabu, bali neno liumizalo huchochea hasira.
2 Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
Ulimi wa mwenye hekima husifu maarifa, bali kinywa cha mpumbavu hufoka upumbavu.
3 Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
Macho ya Bwana yako kila mahali, yakiwaangalia waovu na wema.
4 Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
Ulimi uletao uponyaji ni mti wa uzima, bali ulimi udanganyao huponda roho.
5 Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
Mpumbavu hubeza maonyo ya baba yake, bali yeyote akubaliye maonyo huonyesha busara.
6 Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
Nyumba ya mwenye haki ina hazina kubwa, bali mapato ya waovu huwaletea taabu.
7 Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
Midomo ya mwenye hekima hueneza maarifa, bali sivyo ilivyo mioyo ya wapumbavu.
8 Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
Bwana huchukia sana dhabihu za waovu, bali maombi ya wanyofu humfurahisha Mungu.
9 Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
Bwana huchukia sana njia ya waovu, bali huwapenda wale wafuatao haki.
10 Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
Adhabu kali humngoja yeye aachaye njia; yeye achukiaye maonyo atakufa.
11 Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol h7585)
Mauti na Uharibifu viko wazi mbele za Bwana: je, si zaidi sana mioyo ya wanadamu! (Sheol h7585)
12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
Mwenye mzaha huchukia maonyo; hatataka shauri kwa mwenye hekima.
13 Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
Moyo wenye furaha hufanya uso uchangamke, bali maumivu ya moyoni huponda roho.
14 Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
Moyo wa mwenye ufahamu hutafuta maarifa, bali kinywa cha mpumbavu hujilisha upumbavu.
15 Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
Siku zote za wanaoonewa ni za taabu, bali moyo mchangamfu una karamu ya kudumu.
16 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
Afadhali kuwa na kidogo pamoja na kumcha Bwana, kuliko mali nyingi pamoja na ghasia.
17 Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
Afadhali chakula cha mboga mahali palipo na upendo kuliko nyama ya ndama iliyonona pamoja na chuki.
18 Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
Mtu mwepesi wa hasira huchochea ugomvi, bali mtu mvumilivu hutuliza ugomvi.
19 Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
Njia ya mvivu imezibwa na miiba, bali njia ya mwenye haki ni barabara kuu.
20 Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
Mwana mwenye hekima huleta furaha kwa baba yake, bali mtu mpumbavu humdharau mama yake.
21 Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
Upumbavu humfurahisha mtu ambaye hana akili, bali mtu mwenye ufahamu hushika njia iliyonyooka.
22 Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
Mipango hushindwa kufanikiwa kwa ajili ya kukosa ushauri, bali kukiwa na washauri wengi hufanikiwa.
23 Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
Mtu hupata furaha katika kutoa jibu linalofaa: je, ni zuri namna gani neno lililotoka kwa wakati wake!
24 Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol h7585)
Mapito ya uzima huelekea juu kwa ajili ya wenye hekima kumwepusha asiende chini kaburini. (Sheol h7585)
25 Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
Bwana hubomoa nyumba ya mtu mwenye kiburi, bali huilinda mipaka ya mjane isiguswe.
26 Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
Bwana huchukia sana mawazo ya mwovu, bali mawazo ya wale walio safi humfurahisha yeye.
27 Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
Mtu mwenye tamaa huletea jamaa yake taabu, bali yeye achukiaye rushwa ataishi.
28 Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
Moyo wa mwenye haki hupima majibu yake, bali kinywa cha mwovu hufoka ubaya.
29 Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
Bwana yuko mbali na waovu, bali husikia maombi ya wenye haki.
30 Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
Mtazamo wa tabasamu huleta furaha moyoni, nazo habari njema huipa mifupa afya.
31 Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
Yeye asikilizaye maonyo yatoayo uzima atakuwa miongoni mwa wenye hekima.
32 Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
Yeye anayedharau maonyo hujidharau mwenyewe, bali yeyote anayekubali maonyo hupata ufahamu.
33 Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.
Kumcha Bwana humfundisha mtu hekima, nao unyenyekevu huja kabla ya heshima.

< Miyambo 15 >