< Miyambo 15 >
1 Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
La respuesta suave quita la ira; mas la palabra áspera hace subir el furor.
2 Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
La lengua de los sabios adornará la sabiduría; mas la boca de los locos hablará locura.
3 Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
Los ojos del SEÑOR están en todo lugar, mirando a los malos y a los buenos.
4 Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
La sana lengua es árbol de vida; mas la perversidad en ella es una brecha en el espíritu.
5 Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
El loco menosprecia el castigo de su padre; mas el que guarda la corrección, saldrá cuerdo.
6 Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
En la casa del justo hay gran provisión; pero turbación en los frutos del impío.
7 Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
Los labios de los sabios esparcen sabiduría; mas no así el corazón de los locos.
8 Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
El sacrificio de los impíos es abominación al SEÑOR; mas la oración de los rectos es su gozo.
9 Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
Abominación es al SEÑOR el camino del impío; mas él ama al que sigue justicia.
10 Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
El castigo es molesto al que deja el camino; mas el que aborreciere la corrección, morirá.
11 Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol )
El infierno y la perdición están delante del SEÑOR; ¡cuánto más los corazones de los hombres! (Sheol )
12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
El burlador no ama al que le corrige; ni se allega a los sabios.
13 Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
El corazón alegre hermosea el rostro; mas por el dolor de corazón el espíritu se abate.
14 Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
El corazón entendido busca la sabiduría; mas la boca de los locos pace locura.
15 Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
Todos los días del pobre son trabajosos; mas el de buen corazón tiene un convite continuo.
16 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
Mejor es lo poco con el temor del SEÑOR, que el gran tesoro donde hay turbación.
17 Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
Mejor es la comida de legumbres donde hay amor, que de buey engordado donde hay odio.
18 Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
El hombre iracundo revolverá contiendas; mas el que tarde se enoja, apaciguará la rencilla.
19 Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
El camino del perezoso es como seto de espinos; mas la vereda de los rectos como una calzada.
20 Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
El hijo sabio alegra al padre; mas el hombre loco menosprecia a su madre.
21 Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
La locura es alegría al falto de entendimiento; mas el hombre entendido enderezará su caminar.
22 Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
Los pensamientos son frustrados donde no hay consejo; mas en la multitud de consejeros se afirman.
23 Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
El hombre se alegra con la respuesta de su boca; y la palabra a su tiempo, ¡cuán buena es!
24 Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol )
El camino de la vida es cuesta arriba al entendido, para apartarse del infierno abajo. (Sheol )
25 Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
El SEÑOR asolará la casa de los soberbios; mas él afirmará la heredad de la viuda.
26 Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
Abominación son al SEÑOR los pensamientos del malo; mas el hablar de los limpios es limpio.
27 Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
Alborota su casa el codicioso; mas el que aborrece las dádivas vivirá.
28 Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
El corazón del justo piensa para responder; mas la boca de los impíos derrama malas cosas.
29 Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
Lejos está el SEÑOR de los impíos; mas él oye la oración de los justos.
30 Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
La luz de los ojos alegra el corazón; y la buena fama engorda los huesos.
31 Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
La oreja que escucha la corrección de vida, entre los sabios morará.
32 Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
El que tiene en poco el castigo, menosprecia su alma; mas el que escucha la corrección, tiene corazón entendido.
33 Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.
El temor del SEÑOR es enseñanza de sabiduría; y delante de la honra está la humildad.