< Miyambo 15 >

1 Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
Odpověd měkká odvracuje hněv, ale řeč zpurná vzbuzuje prchlivost.
2 Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
Jazyk moudrých ozdobuje umění, ale ústa bláznů vylévají bláznovství.
3 Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
Na všelikém místě oči Hospodinovy spatřují zlé i dobré.
4 Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
Zdravý jazyk jest strom života, převrácenost pak z něho ztroskotání od větru.
5 Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
Blázen pohrdá cvičením otce svého, ale kdož ostříhá naučení, opatrnosti nabude.
6 Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
V domě spravedlivého jest hojnost veliká, ale v úrodě bezbožného zmatek.
7 Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
Rtové moudrých rozsívají umění, srdce pak bláznů ne tak.
8 Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
Obět bezbožných ohavností jest Hospodinu, ale modlitba upřímých líbí se jemu.
9 Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
Ohavností jest Hospodinu cesta bezbožného, toho pak, kdož následuje spravedlnosti, miluje.
10 Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
Trestání přísné opouštějícímu cestu, a kdož nenávidí domlouvání, umře.
11 Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol h7585)
Peklo i zatracení jest před Hospodinem, čím více srdce synů lidských? (Sheol h7585)
12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
Nemiluje posměvač toho, kterýž ho tresce, aniž k moudrým přistoupí.
13 Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
Srdce veselé obveseluje tvář, ale pro žalost srdce duch zkormoucen bývá.
14 Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
Srdce rozumného hledá umění, ale ústa bláznů pasou se bláznovstvím.
15 Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
Všickni dnové chudého zlí jsou, ale dobromyslného hody ustavičné.
16 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
Lepší jest maličko s bázní Hospodinovou než poklad veliký s nepokojem.
17 Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
Lepší jest krmě z zelí, kdež jest láska, nežli z krmného vola, kdež jest nenávist.
18 Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
Muž hněvivý vzbuzuje sváry, ale zpozdilý k hněvu upokojuje svadu.
19 Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
Cesta lenivého jest jako plot z trní, ale stezka upřímých jest vydlážená.
20 Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
Syn moudrý obveseluje otce, bláznivý pak člověk pohrdá matkou svou.
21 Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
Bláznovství jest veselím bláznu, ale člověk rozumný upřímo kráčeti směřuje.
22 Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
Kdež není rady, zmařena bývají usilování, ale množství rádců ostojí.
23 Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
Vesel bývá člověk z odpovědi úst svých; nebo slovo v čas příhodný ó jak jest dobré!
24 Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol h7585)
Cesta života vysoko jest rozumnému proto, aby se uchýlil od pekla dole. (Sheol h7585)
25 Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
Dům pyšných vyvrací Hospodin, meze pak vdovy upevňuje.
26 Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
Ohavností jsou Hospodinu myšlení zlého, ale čistých řeči vzácné.
27 Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
Kdož dychtí po lakomství, kormoutí dům svůj; ale kdož nenávidí darů, živ bude.
28 Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
Srdce spravedlivého přemyšluje, co má mluviti, ale ústa bezbožných vylévají všelijakou zlost.
29 Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
Vzdálen jest Hospodin od bezbožných, ale modlitbu spravedlivých vyslýchá.
30 Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
To, což se zraku naskýtá, obveseluje srdce; pověst dobrá tukem naplňuje kosti.
31 Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
Ucho, kteréž poslouchá trestání života, u prostřed moudrých bydliti bude.
32 Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
Kdo se vyhýbá cvičení, zanedbává duše své; ale kdož přijímá domlouvání, má rozum.
33 Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.
Bázeň Hospodinova jest cvičení se moudrosti, a slávu předchází ponížení.

< Miyambo 15 >