< Miyambo 15 >
1 Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
Мек отговор отклонява ярост, А оскърбителната дума възбужда гняв.
2 Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
Езикът на мъдрите изказва знание, А устата на безумните изригват глупост.
3 Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
Очите Господни са на всяко място И наблюдава злите и добрите.
4 Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
Благият език е дърво на живот, А извратеността в него съкрушава духа.
5 Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
Безумният презира поуката на баща си, Но който внимава в изобличението, е благоразумен.
6 Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
В дома на праведния има голямо изобилие, А в доходите на нечестивия има загриженост.
7 Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
Устните на мъдрите разсяват знание, А сърцето на безумните не прави така.
8 Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
Жертвата на нечестивите е мерзост Господу, А молитвата на праведните е приятна Нему.
9 Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
Пътят на нечестивия е мерзост Господу, Но Той обича този, който следва правдата.
10 Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
Има тежко наказание за ония, които се отбиват от пътя; И който мрази изобличение ще умре.
11 Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol )
Адът и погибелта са открити пред Господа, - Колко повече сърцата на човешките чада! (Sheol )
12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
Присмивателят не обича изобличителя си, Нито ще отива при мъдрите.
13 Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
Весело сърце прави засмяно лице, А от скръбта на сърцето духът се съкрушава.
14 Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
Сърцето на разумния търси знание А устата на безумните се хранят с глупост.
15 Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
За наскърбения всичките дни са зли А оня, който е с весело сърце, има всегдашно пируване.
16 Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
По-добро е малкото със страх от Господа, Нежели много съкровища с безпокойствие.
17 Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
По-добра е гощавката от зеле с любов, Нежели хранено говедо с омраза.
18 Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
Яростният човек подига препирни, А който скоро не се гневи усмирява крамоли.
19 Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
Пътят на ленивия е като трънен плет, А пътят на праведните е като друм.
20 Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
Мъдър син радва баща си, А безумен човек презира майка си.
21 Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
На безумния глупостта е радост, А разумен човек ходи по прав път.
22 Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
Дето няма съвещание намеренията се осуетяват, А в множеството на съветниците те се утвърждават.
23 Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
От отговора на устата си човек изпитва радост, И дума на време казана, колко е добра!
24 Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol )
За разумния пътят на живота върви нагоре, За да се отклони от ада долу. (Sheol )
25 Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
Господ съсипва дома на горделивите, А утвърдява предела на вдовицата.
26 Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
Лошите замисли са мерзост Господу! А чистите думи Му са угодни.
27 Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
Користолюбивият смущава своя си дом, А който мрази даровете ще живее.
28 Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
Сърцето на праведния обмисля що да отговаря, А устата на нечестивите изригват зло.
29 Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
Господ е далеч от нечестивите, А слуша молитвата на праведните.
30 Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
Светъл поглед весели сърцето, И добри вести угояват костите.
31 Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
Ухо, което слуша животворното изобличение, Ще пребивава между мъдрите.
32 Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
Който отхвърля поуката презира своята си душа, А който слуша изобличението придобива разум.
33 Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.
Страхът от Господа е възпитание в мъдрост, И смирението предшествува славата.