< Miyambo 14 >

1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
Ɔbea nyansafo si ne dan, nanso ɔbea kwasea de nʼankasa ne nsa dwiriw ne de gu fam.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
Nea ne nantew teɛ no suro Awurade, na nea nʼakwan kyea no bu no animtiaa.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
Ɔkwasea kasa ma wɔbɔ nʼakyi abaa, nanso anyansafo ano bɔ wɔn ho ban.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Faako a anantwi nni no, adididaka no mu da mpan, na nantwi ahoɔden mu na nnɔbae pii fi ba.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
Ɔdanseni nokwafo rennaadaa, ɔdansekurumni hwie atoro gu hɔ.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
Ɔfɛwdifo hwehwɛ nyansa nanso onya, nanso wɔn a wɔwɔ nhumu nya nimdeɛ ntɛm.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Twe wo ho fi ɔkwasea ho, efisɛ, worennya nimdeɛ mfi nʼano.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
Anitewfo nyansa ne sɛ wɔbɛdwene wɔn akwan ho, na nkwaseafo agyimisɛm yɛ nnaadaa.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
Nkwaseafo de bɔne ho adwensakra di fɛw, na wɔn a wɔteɛ mu na anisɔ wɔ.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
Koma biara nim ɔyaw wɔ ne mu, na obi foforo rentumi ne no nkyɛ nʼanigye.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
Wɔbɛsɛe amumɔyɛfo fi, nanso teefo ntamadan bɛyɛ frɔmfrɔm.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
Ɔkwan bi wɔ hɔ a ɛteɛ wɔ onipa ani so, nanso awiei no, ɛkɔ owu mu.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Ɔserew mu mpo, koma tumi di yaw, na anigye tumi wie awerɛhow.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
Akyirisanfo benya akatua sɛnea wɔn akwan te, na onipa pa nso benya ne de.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
Atetekwaa gye biribiara di, nanso onitefo dwene nʼanammɔntu ho.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
Onyansafo suro Awurade na oguan bɔne, nanso ɔkwasea yɛ asowui ne basabasa.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
Onipa a ne bo nkyɛ fuw no yɛ nkwaseade, na wɔtɔn nea ɔpam apam bɔne no.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
Ntetekwaafo agyapade ne gyimi, na wɔde nimdeɛ bɔ anitewfo abotiri.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
Nnipa bɔnefo bɛkotow nnipa pa anim, na amumɔyɛfo akotow atreneefo apon ano.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
Ahiafo de, wɔn yɔnkonom mpo mpɛ wɔn anim ahwɛ, nanso adefo wɔ nnamfonom bebree.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
Nea obu ne yɔnko animtiaa yɛ bɔne, na nhyira nka nea ne yam ye ma ohiani.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
So wɔn a wɔbɔ pɔw bɔne nyera kwan ana? Nanso wɔn a wɔhyehyɛ nea eye no nya adɔe ne nokware.
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
Adwumadenyɛ nyinaa de mfaso ba, na kasahunu de, ɛkɔ ohia mu.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
Anyansafo ahonya ne wɔn abotiri, na nkwaseafo agyimisɛm sow gyimi aba.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
Ɔdanseni nokwafo gye nkwa, nanso ɔdansekurumni yɛ ɔdaadaafo.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
Nea osuro Awurade no wɔ bammɔ a mu yɛ den, na ɛbɛyɛ guankɔbea ama ne mma.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
Awurade suro yɛ nkwa asuti, eyi onipa fi owu afiri mu.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
Ɔman mu nnipa dodow yɛ ɔhene anuonyam, nanso sɛ asomfo nni hɔ a mmapɔmma no sɛe.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
Onipa a ɔwɔ abodwokyɛre wɔ ntease a mu dɔ, na nea ne bo fu ntɛm no da agyimisɛm adi.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
Koma mu asomdwoe ma nipadua nkwa, na anibere ma nnompe porɔw.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
Nea ɔhyɛ ahiafo so no bu wɔn Yɛfo animtiaa, nanso nea ohu ohiani mmɔbɔ no hyɛ Onyankopɔn anuonyam.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
Sɛ amanehunu ba a amumɔyɛfo hwe ase, nanso owu mu mpo atreneefo wɔ guankɔbea.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
Nyansa te ntease koma mu, na nkwaseafo mu mpo, oyi ne ho adi.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Trenee pagyaw ɔman, na bɔne yɛ animguase ma nnipa nyinaa.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
Ɔhene ani sɔ ɔsomfo nyansani, na ɔsomfo nimguasefo hyɛ no abufuw.

< Miyambo 14 >