< Miyambo 14 >
1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
La mujer sabia construye su casa; pero la mujer necia, la derriba con sus propias manos.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
Los que viven en rectitud respetan al Señor, pero los que viven con deshonestidad lo aborrecen.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
Las palabras de los tontos herirán su orgullo, pero las palabras de los sabios los protegerán.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Sin bueyes, el pesebre esta vacío; pero una buena cosecha es el fruto de la fuerza de un buey.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
Un testigo fiel no miente, pero un testigo falso es engañoso.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
Para el burlador no tiene sentido buscar la sabiduría, pero el conocimiento llega al que entiende.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Aléjate de los necios, porque no aprenderás nada de ellos.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
Los prudentes usan su sabiduría para decidir hacia donde van; pero la estupidez de los necios traicionera.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
Los necios se burlan del pecado, pero los justos anhelan el perdón.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
Solo la mente del individuo conoce su propia tristeza; y nadie más puede compartir su alegría.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
La casa de los malvados será destruida, pero la tienda de los justos prosperará.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
Hay camino que parece bueno pero al final es camino de muerte.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Incluso mientras ríes puedes estar sintiendo tristeza. La alegría puede terminar en llanto.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
Las personas desleales reciben el pago por sus actos, pero los justos son recompensados.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
Los necios creen cualquier cosa que les dicen, pero los prudentes piensan en lo que hacen.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
Los sabios son cuidadosos y evitan el mal, pero los necios andan confiados en su imprudencia.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
Los irascibles actúan con necedad, mientras que los que conspiran maldad son odiados.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
La herencia de los tontos es la estupidez, pero los imprudentes son recompensados con conocimiento.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
Los malvados se inclinan ante los justos, y se arrodillan a las puertas de los justos.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
Los pobres son aborrecidos incluso por sus vecinos, mientras que los ricos tienen muchos amigos.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
Los que menosprecian a sus vecinos son pecadores, pero los que son bondadosos con los pobres son bendecidos.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
¿Acaso no está mal conspirar para hacer maldad? Pero los que piensan en hacer el bien tienen amor y fidelidad.
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
Hay recompensa en el trabajo arduo, pero el mucho hablar solo trae pobreza.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
Los sabios son recompensados con riqueza, pero los necios reciben estupidez como pago.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
Un testigo verdadero salva vidas, pero el testigo falso es traicionero.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
Los que honran al Señor están a salvo; el protegerá a sus hijos.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
Respetar al Señor es fuente de vida con la cual puedes evadir las trampas de la muerte.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
La gloria de un rey es la cantidad de súbditos que tiene, porque un gobernante no es nadie sin ellos.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
Si eres tardo para enojarte, eres sabio; pero si te enojas con facilidad, glorificas la estupidez.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
Una mente en paz ayuda a la salud de tu cuerpo; pero los celos hacen podrir los huesos.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
Todo el que oprime al pobre insulta a su Creador; pero todo el que los trata con bondad da honra a su Hacedor.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
Los malvados son derribados por sus propias acciones, pero los que viven en rectitud están confiados hasta la muerte.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
La sabiduría habita en una mente que entiende, pero no se encuentra en medio de los necios.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Hacer el bien dará éxito a la nación, pero el pecado causa desgracia a cualquier pueblo.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
El siervo que actúa con sabiduría es estimado por el rey; pero el rey se enojará con el siervo que actúa vergonzosamente.