< Miyambo 14 >

1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
Wonke owesifazana ohlakaniphileyo uyayakha indlu yakhe, kodwa oyisithutha uyayidiliza ngezandla zakhe.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
Ohamba ngobuqotho bakhe wesaba iNkosi, kodwa ophambene ngendlela zakhe uyayidelela.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
Emlonyeni wesithutha kulentonga yokuzigqaja, kodwa indebe zabahlakaniphileyo ziyabagcina.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Lapho okungekho izinkabi khona umkolo uhlanzekile, kodwa kulesivuno esinengi ngamandla enkabi.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
Umfakazi othembekileyo kaqambi amanga, kodwa umfakazi wamanga uphafuza amanga.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
Odelelayo udinga inhlakanipho, kodwa kayikho; kodwa ulwazi lulula koqedisisayo.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Suka phambi komuntu oyisithutha, nxa ungayikunanzelela kuye indebe zolwazi.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
Inhlakanipho yokhaliphileyo yikuqedisisa indlela yakhe, kodwa ubuthutha bezithutha buyinkohliso.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
Izithutha ziyakloloda ngesono, kodwa phakathi kwabaqotho kulomusa.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
Inhliziyo iyazi ukubaba kwayo ngokwayo, lowemzini kahlanganyeli lentokozo yayo.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
Indlu yabakhohlakeleyo izachithwa, kodwa ithente labaqotho lizahluma.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
Kukhona indlela ebonakala ilungile emuntwini, kodwa ukuphela kwayo zindlela zokufa.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Lekuhlekeni inhliziyo isebuhlungwini, lokuphela kwaleyontokozo lusizi.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
Ohlehlela nyovane ngenhliziyo uzasutha ngezindlela zakhe, kodwa umuntu olungileyo uzasutha ngaye ngokwakhe.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
Ongelalwazi ukholwa lonke ilizwi, kodwa olengqondo unanzelela ukuhamba kwakhe.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
Ohlakaniphileyo uyesaba, asuke ebubini, kodwa isithutha siyathukuthela, silitshapha.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
Ophangisa ukuthukuthela wenza ubuthutha, lomuntu wamacebo amabi uzazondwa.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
Abangelalwazi badla ilifa lobuthutha, kodwa abakhaliphileyo bazathwala umqhele wolwazi.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
Ababi bakhothama phambi kwabalungileyo, labakhohlakeleyo emasangweni abalungileyo.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
Umyanga uzondwa langumakhelwane wakhe, kodwa abathanda onothileyo banengi.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
Odelela umakhelwane wakhe uyona, kodwa olomusa kubayanga ubusisiwe.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
Kabaduhi yini abaceba okubi? Kodwa umusa leqiniso ngokwalabo abaceba okuhle.
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
Kumtshikatshika wonke kulenzuzo, kodwa inkulumo yendebe ibanga inswelo kuphela.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
Umqhele wabahlakaniphileyo uyinotho yabo; ubuthutha bezithutha buyibuthutha.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
Umfakazi oqinisileyo uyophula imiphefumulo, kodwa ophafuza amanga ungumkhohlisi.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
Ekuyesabeni iNkosi kulethemba eliqinileyo, labantwana bakhe bazakuba lesiphephelo.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
Ukuyesaba iNkosi kungumthombo wempilo, ukusuka emijibileni yokufa.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
Lusebunengini babantu udumo lwenkosi, kodwa kusekuswelekeni kwabantu ukuchitheka kombusi.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
Ophuza ukuthukuthela ulokuqedisisa okukhulu, kodwa ophangisa ukuzonda ukhulisa ubuthutha.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
Inhliziyo ephilileyo iyimpilo yenyama, kodwa umhawu uyikubola kwamathambo.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
Ocindezela umyanga uthuka uMenzi wakhe, kodwa olomusa koswelayo uyamdumisa.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
Okhohlakeleyo uwiswa ebubini bakhe, kodwa olungileyo ulethemba ekufeni kwakhe.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
Inhlakanipho ihlala enhliziyweni yoqedisisayo, kodwa okuphakathi kwezithutha kuyaziwa.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Ukulunga kuphakamisa isizwe, kodwa isono silihlazo ebantwini.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
Umusa wenkosi usencekwini ehlakaniphileyo, kodwa intukuthelo yayo izakuba kwethela ihlazo.

< Miyambo 14 >