< Miyambo 14 >
1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
Umfazi ohlakaniphileyo uyakha indlu yakhe, kodwa lowo oyisiwula uyayibhidliza ngezandla zakhe.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
Lowo ohamba ngobuqotho uyamesaba uThixo, kodwa lowo ondlela zakhe zigobile uyameyisa.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
Inkulumo yesiwula isikhothisa ngoswazi emhlane, kodwa indebe zalowo ohlakaniphileyo ziyamvikela.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Lapho okungelankabi khona isibaya siyize, kodwa amandla enkabi aletha isivuno esinengi.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
Umfakazi oleqiniso kakhohlisi, kodwa umfakazi ongelaqiniso uhutsha amanga.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
Oweyisayo uyakudinga ukuhlakanipha kodwa kakutholi, kodwa ulwazi luyazizela koqondisisayo.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Suka emuntwini oyisiwula, ngoba awuyikuthola ulwazi ezindebeni zakhe.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
Ukuhlakanipha kwabaqondayo yikuthi bayacabanga ngalokho abakwenzayo, kodwa ubuthutha beziwula buyinkohliso.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
Iziwula zikwenza ubuthutha ukuphenduka ezonweni, kodwa abaqotho bafisa ukwenza uxolo.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
Inhliziyo leyo laleyo iyakwazi ukudabuka kwayo, njalo kakho ongakwazi ukuthokoza kwayo.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
Indlu yomubi izadilizwa, kodwa ithente loqotho lizaphumelela.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
Kukhona indlela ebonakala ilungile emuntwini, kodwa isiphetho sayo siyikufa.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Ukuhleba kungabe kufihle ubuhlungu benhliziyo, lokuthokoza kucine sekulusizi.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
Abangelakho bazavuzwa ngokubafaneleyo, lomuntu olungileyo laye avuzwe ngokwakhe.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
Umuntu oyisithutha ukholwa loba yini, kodwa olengqondo uyakucabangisisa konke akwenzayo.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
Umuntu ohlakaniphileyo uyamesaba uThixo, axwaye okubi, kodwa isiwula siliphikankani kodwa sizizwa sivikelekile.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
Umuntu olicaphucaphu wenza izinto zobuthutha, lomuntu oliqili uyazondwa.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
Abangazi lutho ilifa labo yibuwula, kodwa abalengqondo betheswa umqhele wolwazi.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
Abantu ababi bazilahla phansi phambi kwabalungileyo, lezixhwali ziguqa emasangweni abalungileyo.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
Abayanga bahlanyukelwa langabomakhelwane babo, kodwa izinothi zilabangane abanengi.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
Lowo oweyisa umakhelwane wenza isono, kodwa ubusisiwe olomusa kwabaswelayo.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
Kabalahleki yini abaceba ububi? Kodwa abamisa ukwenza okuhle bafumana uthando lokuthembeka.
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
Ukusebenza nzima konke kuletha inzuzo, kodwa ukuqina ngomlomo kuthelela ubuyanga.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
Inotho yabahlakaniphileyo ingumqhele wabo, kodwa ubuphukuphuku beziwula buzala ubuthutha.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
Umfakazi oleqiniso uyabakhulula abantu, kodwa umfakazi wamanga uyakhohlisa.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
Lowo owesaba uThixo ulenqaba eqinileyo, uzakuba yisiphephelo senzalo yakhe.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
Ukumesaba uThixo kungumthombo wokuphila, kuvikela umuntu emijibileni yokufa.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
Ubunengi babantu elizweni kuludumo enkosini, kodwa nxa kungelabantu umbusi kasilutho.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
Umuntu obekezelayo uyazwisisa kakhulu, kodwa ophanga ukuthukuthela uveza ubuthutha.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
Ingqondo elokuthula iletha ukuphila emzimbeni, kodwa umhawu ubolisa amathambo.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
Lowo oncindezela abayanga weyisa uMenzi wabo, kodwa olomusa kwabaswelayo udumisa uNkulunkulu.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
Nxa kufika ubunzima ababi bayadilika, kodwa abalungileyo balesiphephelo lasekufeni.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
Ukuhlakanipha kuzinzile enhliziyweni yabaqedisisayo, kuyaziveza kanye lakwabayiziwula.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Ukulunga kuyasiphakamisa isizwe, kodwa isono silihlazo lakubaphi abantu.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
Inkosi iyathokoza ngenceku ehlakaniphileyo, kodwa inceku ehlazisayo iyayithukuthelisa.