< Miyambo 14 >
1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
Az asszonyok legbölcsebbike fölépítette házát, de az oktalanság önkezeivel lerontja.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
Egyenességében jár, a ki az Örökkévalót féli, de álnok az útjain, a ki őt megveti.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
Az oktalannak szájában a gőgnek vesszeje van, de a bölcsek ajkai megőrzik őket,
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Ökrök híján tiszta a jászol, de termések bősége a marha erejében van.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
Hűséges tanú nem hazudik, de hazugságokat terjeszt hazug tanú.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
Keresett a csúfoló bölcsességet, de nincs, az értelmesnek azonban könnyű a tudás.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Menj el a balga ember közeléből, és nem ismerted meg tudásnak ajkait,
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
Az okosnak bölcsessége: érteni az útját, de a balgák oktatalansága csalárdság.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
Az oktalanok közt tolmács a bűn és az egyenesek közt a jóakarat.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
A szív ismeri önmagának keservét, és örömébe nem vegyül idegen.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
A gonoszok háza megsemmisül, de az egyenesek sátra virul.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
Van út, mely egyenes az ember előtt, de a vége – halálnak útjai.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Nevetés közt is fájhat a szív, és az örömnek vége bánat.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
Saját útjaiból lakik jól a tévedt szívű, az övéiből a jó ember.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
Az együgyű minden szónak hisz, de az okos ügyel lépésére.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
A bölcs fél és kerüli a rosszat, de a balga fölháborodik és elbizakodik.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
A hirtelen haragú oktalanságot követ el, és a fondorlatok embere meggyűlöltetik.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
Birtokul nyertek az együgyűek oktalanságot, de az okosok körülfogják a tudást.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
Legörnyedtek a rosszak a jók előtt és a gonoszok az igaznak kapuinál.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
Társánál is gyűlöletessé válik a szegény, de a gazdagnak barátai sokan vannak.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
A ki gúnyolódik felebarátján, vétkezik, de a ki könyörül a szegényeken, boldog az.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
Nemde eltévelyegnek a rosszat koholók, de szeretetet és hűséget találnak a jót koholók.
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
Minden fáradalomból nyereség származik, de az ajkak beszédje csak hiányra visz.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
A bölcsek koronája a gazdagságuk, a balgák oktalansága oktalanság.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
Lelkeket ment meg az igaz tanú, de hazugságokat terjeszt a csalárd.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
Az istenfélelemben erős bizalom van, fiainak is menedékük lesz.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
Az istenfélelem életforrás, hogy távozzunk a halál tőreitől.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
Abban, hogy sok a nép, van a király dísze, és a nemzet fogytában a fejedelem rettegése.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
A késedelmes haragú nagy értelmességű, de a hirtelen indulatú oktalanságot visz el.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
A testnek élete a szelíd szív, de a csontok rothadása a vakbuzgalom.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
A ki nyomorgatja a szegényt, az káromolta alkotóját, de tiszteli őt, a ki könyörül a szűkölködőn.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
Szerencsétlenségében eltaszíttatik a gonosz, de halálakor is bízik az igaz.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
Az értelmesnek szívében bölcsesség nyugszik, de a balgák közepében kitudódik.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Igazság felemeli a nemzetet, de a népek gyalázata a vétek.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
A király jóakarata az eszes szolgáé, de haragja lesz a szégyenletesé.