< Miyambo 14 >
1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
Une femme sage édifie sa maison; l’insensée détruira de ses propres mains celle même qui était construite.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
Celui qui marche par un droit chemin, et qui craint le Seigneur, est méprisé par celui qui marche dans une voie infâme.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
Dans la bouche d’un insensé est la verge de l’orgueil; mais les lèvres des sages les gardent.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Où il n’y a point de bœufs, la crèche est vide; mais où abondent les moissons, là est manifeste la force du bœuf.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
Un témoin fidèle ne ment pas, mais un témoin trompeur profère le mensonge.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
Le railleur cherche la sagesse, et ne la trouve pas: la doctrine des prudents est facile.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Va contre l’homme insensé, et qui ne connaît pas les lèvres de la prudence.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
La sagesse d’un homme habile est de comprendre sa voie; et l’imprudence des insensés est errante.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
L’insensé se jouera du péché; et c’est parmi les justes que demeurera la grâce.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
Quant au cœur qui connaît l’amertume de son âme, un étranger ne se mêlera pas dans sa joie.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
La maison des impies sera détruite; mais les tabernacles des justes seront florissants.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
Il est une voie qui paraît droite à l’homme; mais ses issues conduisent à la mort.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Le rire de douleur sera mêlé, et le deuil occupe les extrémités de la joie.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
L’insensé sera rempli de ses voies; mais au-dessus de lui sera l’homme vertueux.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
L’innocent croit à toute parole: l’homme avisé considère ses pas. Pour un fils trompeur il n’y aura rien de bon: mais à un serviteur sage ses actes seront prospères, et sa voie sera dirigée.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
Le sage craint et se détourne du mal: l’insensé passe outre et a confiance.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
L’impatient commettra des actions de folie; l’homme artificieux est odieux.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
Les tout petits posséderont la folie; et les hommes avisés attendront la science.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
Les méchants seront couchés par terre devant les bons; et les impies devant les portes des justes.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
Même à son prochain, le pauvre est odieux; mais les amis des riches sont nombreux.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
Celui qui méprise son prochain pèche; mais celui qui a pitié du pauvre sera bienheureux. Celui qui croit au Seigneur aime la miséricorde.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
Ils s’égarent, ceux qui opèrent le mal: la miséricorde et la vérité préparent des biens.
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
Dans tout travail sera l’abondance: mais où il y a beaucoup de paroles, là fréquemment est la détresse.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
La couronne des sages, ce sont leurs richesses; la sottise des insensés, l’imprudence.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
Un témoin fidèle délivre des âmes: et celui qui est double profère des mensonges.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
Dans la crainte du Seigneur est une confiance ferme; et à ses enfants sera l’espérance.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
La crainte du Seigneur est une source de vie, afin qu’on évite la ruine de la mort.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
Dans la multitude du peuple est la gloire d’un roi; et dans le petit nombre des sujets l’ignominie d’un prince.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
Celui qui est patient se gouverne avec une grande prudence; mais celui qui est impatient signale sa folie.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
La vie des chairs, c’est la santé du cœur: la carie des os, l’envie.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
Celui qui opprime un indigent, outrage le créateur de cet indigent; mais celui-là l’honore, qui a pitié d’un pauvre.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
À cause de sa malice, l’impie sera rejeté; mais le juste espère dans sa mort même.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
Dans le cœur de l’homme prudent repose la sagesse; et elle instruira tous les ignorants.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
La justice élève une nation; mais le péché fait les peuples malheureux.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
Un ministre intelligent est bien accueilli du roi; celui qui est inutile endurera son courroux.