< Miyambo 14 >
1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
The wise woman buildeth her house; But the foolish teareth it down with her hands.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
He who walketh in uprightness feareth the LORD; But he who is perverse in his ways despiseth him.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
In the mouth of the foolish pride is a scourge; But the lips of the wise preserve them.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Where there are no oxen, the crib is clean; But there is great increase by the strength of the ox.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
A faithful witness doth not lie; But a false witness poureth forth lies.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
The scoffer seeketh wisdom, and findeth it not; But knowledge is easy to the man of understanding.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Go from the presence of a foolish man; For thou hast not perceived in him the lips of knowledge.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
The wisdom of the prudent is in giving heed to his way; But the folly of fools is deceit.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
Fools make a mock at sin; But with the upright is favor.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
The heart knoweth its own bitterness. And a stranger cannot intermeddle with its joy.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
The house of the wicked shall be destroyed; But the tent of the upright shall flourish.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
There is a way which seemeth right to a man, But its end is the way to death.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Even in laughter the heart is sorrowful, And the end of joy is grief.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
The perverse in heart shall be filled with his own ways; And from himself shall the good man be satisfied.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
The simple man believeth every word; But the prudent looketh well to his steps.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
The wise man feareth, and departeth from evil; But the fool is haughty and confident.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
He who is hasty in his anger will commit folly; And the man of wicked devices will be hated.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
The simple inherit folly; But the prudent are crowned with knowledge.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
The evil bow before the good; Yea, the wicked at the gates of the righteous.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
The poor is hated even by his own neighbor; But the rich hath many friends.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
He who despiseth his neighbor sinneth; But happy is he who hath mercy on the poor.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
Do not they who devise evil fail of their end? But they who devise good meet with kindness and truth.
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
In all labor there is profit; But the talk of the lips tendeth only to penury.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
Riches are a crown to the wise; But the promotion of fools is folly.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
A true witness saveth lives; But a deceitful witness poureth forth lies.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
In the fear of the LORD is strong confidence; Yea, to his children he will be a refuge.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
The fear of the LORD is a fountain of life; By it men escape from the snares of death.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
In a numerous people is the glory of a king; But the want of people is the destruction of a prince.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
He who is slow to anger is of great understanding. But he who is of a hasty spirit setteth folly on high.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
A quiet heart is the life of the flesh; But the ferment of passion is rottenness to the bones.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
He who oppresseth the poor reproacheth his Maker; But he who hath mercy on the poor honoreth him.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
By his wickedness the wicked is thrust down; But the righteous hath hope even in death.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
Wisdom resteth quietly in the heart of the wise; But in the breast of fools it will be made known.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Righteousness exalteth a people; But the reproach of nations is sin.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
The king's favor is toward a wise servant; But his wrath is against him that causeth shame.