< Miyambo 14 >
1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
A wise woman buildeth her house: but the foolish will pull down with her hands that also which is built.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
He that walketh in the right way, and feareth God, Cis despised by him that goeth by an infamous way.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
In the mouth of a fool is the rod of pride: but the lips of the wise preserve them.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Where there are no oxen, the crib is empty: but where there is much corn, there the strength of the ox is manifest.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
A faithful witness will not lie: but a deceitful witness uttereth a lie.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
A scorner seeketh wisdom, and findeth it not: the learning of the wise is easy.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Go against a foolish man, and he knoweth not the lips of prudence.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
The wisdom of a. discreet man is to understand his way: and the imprudence of fools erreth.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
A fool will laugh at sin, but among the just grace shall abide.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
The heart that knoweth the bitterness of his own soul, in his joy the stranger shall not intermeddle.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
The house of the wicked shall be destroyed: but the tabernacles of the just shall flourish.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
There is a way which seemeth just to a man: but the ends thereof lead to death.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Laughter shall be mingled with sorrow, and mourning taketh hold of the end of joy.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
A fool shall be filled with his own ways, and the good man shall be above him.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
The innocent believeth every word: the discreet man considereth his steps. No good shall come to the deceitful son: but the wise servant shall prosper in his dealings, and his way shall be made straight.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
A wise man feareth and declineth from evil: the fool leapeth over and is confident.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
The impatient man shall work folly: and the crafty man is hateful.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
The childish shall possess folly, and the prudent, shall look for knowledge.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
The evil shall fall down before the good: and the wicked before the gates of the just.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
The poor man shall be hateful even to his own neighbour: but the friends of the rich are many.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
He that despiseth his neighbour, sinneth: but he that sheweth mercy to the poor, shall be blessed. He that believeth in the Lord, loveth mercy.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
They err that work evil: but mercy and truth prepare good things.
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
In much work there shall be abundance: but where there are many words, there is oftentimes want.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
The crown of the wise is their riches: the folly of fools, imprudence.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
A faithful witness delivereth souls: and the double dealer uttereth lies.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
In the fear of the Lord is confidence of strength, and there shall be hope for his children.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
The fear of the Lord is a fountain of life, to decline from the ruin of death.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
In the multitude of people is the dignity of the king: and in the small number of people the dishonour of the prince.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
He that is patient, is governed with much wisdom: but he that is impatient, exalteth his folly.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
Soundness of heart is the life of the flesh: but envy is the rottenness of the bones.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
He that oppresseth the poor, upbraideth his Maker: but he that hath pity on the poor, honoureth him.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
The wicked man shall be driven out in his wickedness: but the just hath hope in his death.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
In the heart of the prudent resteth wisdom, and it shall instruct all the ignorant.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Justice exalteth a nation: but sin maketh nations miserable.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
A wise servant is acceptable to the king: he that is good for nothing shall feel his anger.