< Miyambo 14 >

1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
Kvinders Visdom har bygget sit Hus; men Daarskaben bryder det ned med sine Hænder.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
Den, som vandrer i sin Oprigtighed, frygter Herren; men den, som gaar paa Krogveje, foragter ham.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
I Daarens Mund er Hovmods Ris; men de vises Læber skulle bevare dem selv.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Hvor ingen Øksne ere, der er Krybben ren; men megen Indtægt kommer ved Oksens Kraft.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
Et trofast Vidne lyver ikke; men et falsk Vidne udblæser Løgne.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
Spotteren søger Visdom, og han finder den ikke; men for den forstandige er Kundskab let.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Gak bort fra en Mand, som er en Daare; thi du vil ikke have fundet Kundskab paa hans Læber.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
Den kloges Visdom er, at han forstaar sig paa sin Vej; men Daarers Taabelighed er, at de blive bedragne.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
Daarerne spottes af deres eget Skyldoffer; men med de oprigtige er Velbehageligheden.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
Hjertet kender sin Sjæls Bitterhed, og en fremmed skal ikke blande sig i dets Glæde.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
De ugudeliges Hus skal ødelægges; men de retsindiges Telt skal blomstre.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
Der er en Vej, som kan synes en Mand ret; men til sidst bliver den Vej til Døden.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Selv under Latteren føler Hjertet Smerte, og til sidst bliver Glæden Bedrøvelse.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
Den, hvis Hjerte er afveget, skal mættes ved sine Veje, men den gode Mand ved det, han har i Eje.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
Den uerfarne tror alting, men den kloge agter paa sin Gang.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
Den vise frygter og viger fra ondt; men en Daare er overmodig, og tryg.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
Den, som er hastig til Vrede, gør Daarlighed, og den underfundige Mand hades.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
De uvidende arve Daarlighed; men de kloge favne Kundskab.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
De onde maa bøje sig for de godes Ansigt og de ugudelige for den retfærdiges Porte.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
Selv for sin Ven er den fattige forhadt; men mange ere de, som elske den rige.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
Hvo som foragter sin Næste, synder; men den, som forbarmer sig over de elendige, er lyksalig.
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
Fare ikke de vild, som optænke ondt? men de, som optænke godt, finde Miskundhed og Troskab.
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
I alt besværligt Arbejde er der Fordel; men hvor det bliver ved Læbers Ord, fører det kun til Mangel.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
De vises Rigdom er deres Krone; men Daarers Taabelighed bliver Taabelighed.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
Et sanddru Vidne redder Sjæle, men den, som udblæser Løgn, er svigefuld.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
I Herrens Frygt har en et stærkt Værn, og for hans Børn skal der være en Tilflugt.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
Herrens Frygt er Livets Kilde, saa at man viger fra Dødens Snarer.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
At have meget Folk er en Konges Ære; men hvor Folket er borte, er det en Fyrstes Fordærvelse.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
Den langmodige har megen Forstand; men den, som er hastig i Sindet, forraader Daarskab.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
Et blidt Hjerte er Liv for Legemet; men Hidsighed er Raaddenhed for Benene,
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
Hvo som fortrykker den ringe, forhaaner hans Skaber; men hvo som forbarmer sig over den fattige, ærer ham.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
Den ugudelige styrtes for sin Ondskab; men den retfærdige har Fortrøstning i sin Død.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
I den forstandiges Hjerte hviler Visdommen; men i Daarers Indre giver den sig til Kende.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Retfærdighed ophøjer et Folk; men Synden er Folkenes Skændsel
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
Kongens Velbehag er til en klog Tjener, men hans Vrede er over den, som gør Skam.

< Miyambo 14 >