< Miyambo 13 >

1 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
Mądry syn [przyjmuje] pouczenie ojca, a szyderca nie słucha strofowania.
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
Człowiek będzie spożywać dobro z owocu swoich ust, a dusza przewrotnych [będzie spożywać] przemoc.
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
Kto strzeże swych ust, strzeże swojej duszy; kto [szeroko] otwiera swe wargi, będzie zniszczony.
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
Dusza leniwego pragnie, a nic nie ma, a dusza pracowitych zostanie obficie nasycona.
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
Sprawiedliwy nienawidzi kłamliwego słowa, a niegodziwy staje się obrzydliwy i zhańbiony.
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
Sprawiedliwość strzeże tego, który postępuje uczciwie, a niegodziwość powala grzesznika.
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
Znajduje się taki, który czyni siebie bogatym, a nie ma nic; inny czyni siebie ubogim, choć ma wiele bogactw.
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
Okupem za życie człowieka jest jego bogactwo, a ubogi nie słucha strofowania.
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
Radośnie błyszczy światło sprawiedliwych, a pochodnia niegodziwych zgaśnie.
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
Spór powstaje tylko dzięki pysze, a mądrość jest przy tych, co przyjmują radę.
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
Łatwo zdobyte bogactwo zmniejsza się, a kto je gromadzi [swą] ręką, pomnaża je.
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
Przedłużająca się nadzieja sprawia ból sercu, a spełnione pragnienie [jest] drzewem życia.
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
Kto gardzi słowem [Bożym], ten zginie, a kto się boi przykazania, dostanie nagrodę.
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
Prawo mądrego jest źródłem życia, by uniknąć sideł śmierci.
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
Prawdziwy rozum daje łaskę, a droga przewrotnych jest ciężka.
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
Każdy roztropny postępuje rozważnie, a głupi ujawnia głupotę.
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
Niegodziwy posłaniec popada w zło, a wierny wysłannik jest lekarstwem.
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
Ubóstwo i hańba [spadną na] tego, który odrzuca karność, a kto szanuje upomnienia, dozna czci.
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
Spełnione pragnienie jest słodkie dla duszy, a odwrócenie się od zła budzi odrazę w głupcach.
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
Kto przestaje z mądrymi, będzie mądry, a towarzysz głupców będzie zniszczony.
21 Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
Nieszczęście ściga grzeszników, a sprawiedliwych [Bóg] nagrodzi dobrem.
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
Dobry [człowiek] zostawia dziedzictwo dzieciom [swoich] dzieci, a majątek grzesznika jest zachowany dla sprawiedliwego.
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
Obfita żywność jest na roli ubogich, lecz i ta może niszczeć przez nieroztropność.
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
Kto oszczędza swą rózgę, nienawidzi swego syna, a kto go kocha, karze w porę.
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.
Sprawiedliwy je i syci swoją duszę, a żołądek niegodziwych cierpi niedostatek.

< Miyambo 13 >