< Miyambo 13 >

1 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
پسر حکیم تادیب پدر خود را اطاعت می کند، اما استهزاکننده تهدید رانمی شنود.۱
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
مرد از میوه دهانش نیکویی را می‌خورد، اماجان خیانتکاران، ظلم را خواهد خورد.۲
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
هر‌که دهان خود را نگاه دارد جان خویش رامحافظت نماید، اما کسی‌که لبهای خود رابگشاید هلاک خواهد شد.۳
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
شخص کاهل آرزو می‌کند و چیزی پیدانمی کند. اما شخص زرنگ فربه خواهد شد.۴
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
مرد عادل از دروغ گفتن نفرت دارد، اما شریررسوا و خجل خواهد شد.۵
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
عدالت کسی را که در طریق خود کامل است محافظت می‌کند، اما شرارت، گناهکاران را هلاک می‌سازد.۶
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
هستند که خود را دولتمند می‌شمارند وهیچ ندارند، و هستند که خویشتن را فقیرمی انگارند و دولت بسیار دارند.۷
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
دولت شخص فدیه جان او خواهد بود، امافقیر تهدید را نخواهد شنید.۸
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
نور عادلان شادمان خواهد شد، اما چراغ شریران خاموش خواهد گردید.۹
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
از تکبر جز نزاع چیزی پیدا نمی شود، اما باآنانی که پند می‌پذیرند حکمت است.۱۰
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
دولتی که از بطالت پیدا شود در تناقص می‌باشد، اما هر‌که به‌دست خود اندوزد در تزایدخواهد بود.۱۱
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
امیدی که در آن تعویق باشد باعث بیماری دل است، اما حصول مراد درخت حیات می‌باشد.۱۲
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
هر‌که کلام را خوار شمارد خویشتن راهلاک می‌سازد، اما هر‌که از حکم می‌ترسد ثواب خواهد یافت.۱۳
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
تعلیم مرد حکیم چشمه حیات‌است، تا ازدامهای مرگ رهایی دهد.۱۴
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
عقل نیکو نعمت را می‌بخشد، اما راه خیانتکاران، سخت است.۱۵
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
هر شخص زیرک با علم عمل می‌کند. امااحمق حماقت را منتشر می‌سازد.۱۶
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
قاصد شریر در بلا گرفتار می‌شود، امارسول امین شفا می‌بخشد.۱۷
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
فقر و اهانت برای کسی است که تادیب راترک نماید، اما هر‌که تنبیه را قبول کند محترم خواهد شد.۱۸
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
آرزویی که حاصل شود برای جان شیرین است، اما اجتناب از بدی، مکروه احمقان می‌باشد.۱۹
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
با حکیمان رفتار کن و حکیم خواهی شد، اما رفیق جاهلان ضرر خواهد یافت.۲۰
21 Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
بلا گناهکاران را تعاقب می‌کند، اما عادلان، جزای نیکو خواهند یافت.۲۱
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
مرد صالح پسران پسران را ارث خواهدداد، و دولت گناهکاران برای عادلان ذخیره خواهد شد.۲۲
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
در مزرعه فقیران خوراک بسیار است، اماهستند که از بی‌انصافی هلاک می‌شوند.۲۳
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
کسی‌که چوب را باز‌دارد، از پسر خویش نفرت می‌کند، اما کسی‌که او را دوست می‌دارد اورا به سعی تمام تادیب می‌نماید.۲۴
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.
مرد عادل برای سیری جان خود می‌خورد، اما شکم شریران محتاج خواهد بود.۲۵

< Miyambo 13 >