< Miyambo 13 >

1 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
Indodana ehlakaniphileyo ilalela ukulaya kukayise, kodwa isideleli kasilaleli ukukhuzwa.
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
Umuntu uzakudla okuhle okuvela esithelweni somlomo, kodwa umphefumulo weziphambuki ubudlwangudlwangu.
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
Olondoloza umlomo wakhe ugcina umphefumulo wakhe, kodwa ovula indebe zakhe zibe banzi uzakuba lencithakalo.
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
Umphefumulo wevila uyafisa, kodwa kakulalutho; kodwa umphefumulo wokhutheleyo uyakhuluphaliswa.
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
Olungileyo uyalizonda ilizwi lamanga; kodwa omubi uzenza abe levumba, uthelela ihlazo.
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
Ukulunga kulinda oqotho endleleni, kodwa inkohlakalo ichitha isoni.
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
Kukhona ozitshaya onothileyo, kanti kalalutho; ozitshaya ongumyanga, kanti unothile kakhulu.
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
Inhlawulo yempilo yomuntu yinotho yakhe, kodwa umyanga kezwa ukukhuzwa.
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
Ukukhanya kwabalungileyo kuyathokoza, kodwa isibane sabakhohlakeleyo sizacitshwa.
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
Ukuzigqaja kuveza ingxabano kuphela, kodwa inhlakanipho ikwabalulekiweyo.
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
Inotho etholakala ngokuyize izaphunguka, kodwa obuthelela ngesandla uyayandisa.
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
Ithemba eliphuzayo ligulisa inhliziyo, kodwa isifiso esizayo siyisihlahla sempilo.
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
Odelela ilizwi yena uzachithwa, kodwa owesaba umlayo yena uzavuzwa.
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
Imfundiso yohlakaniphileyo ingumthombo wempilo, ukuthi asuke emijibileni yokufa.
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
Ukuqedisisa okuhle kunika umusa, kodwa indlela yabaphambukayo ilukhuni.
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
Wonke ohlakaniphileyo wenza ngolwazi, kodwa isithutha sichaya ubuthutha.
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
Isithunywa esikhohlakeleyo siwela ebubini, kodwa isithunywa esithembekileyo siyikusilisa.
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
Ubuyanga lehlazo ngokwalowo oyekela ukufundiswa, kodwa onanzelela ukukhuzwa uzadunyiswa.
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
Isifiso esenziweyo simnandi emphefumulweni, kodwa kuyisinengiso ezithutheni ukuphenduka ebubini.
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
Ohamba labahlakaniphileyo uzahlakanipha, kodwa umngane wezithutha uzakuba mubi.
21 Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
Ububi buzazingela izoni, kodwa abalungileyo bazavuzwa ngokuhle.
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
Olungileyo uzabenza abantwana babantwana badle ilifa, kodwa inotho yesoni ibekelwa olungileyo.
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
Ukudla okunengi kusengqathweni yabayanga, kodwa kukhona okukhukhulwa ngokungabi lokwahlulela.
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
Ogodla uswazi lwakhe uzonda indodana yakhe, kodwa oyithandayo uyayidinga masinyane ngesijeziso.
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.
Olungileyo uyadla kuze kusuthe umphefumulo wakhe, kodwa isisu sabakhohlakeleyo sizaswela.

< Miyambo 13 >