< Miyambo 13 >
1 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
Filius sapiens, doctrina patris: qui autem illusor est, non audit cum arguitur.
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
De fructu oris sui homo satiabitur bonis: anima autem praevaricatorum iniqua.
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
Qui custodit os suum, custodit animam suam: qui autem inconsideratus est ad loquendum, sentiet mala.
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
Vult et non vult piger: anima autem operantium impinguabitur.
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
Verbum mendax iustus detestabitur: impius autem confundit, et confundetur.
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
Iustitia custodit innocentis viam: impietas autem peccatorem supplantat.
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
Est quasi dives cum nihil habeat: et est quasi pauper, cum in multis divitiis sit.
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
Redemptio animae viri, divitiae suae: qui autem pauper est, increpationem non sustinet.
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
Lux iustorum laetificat: lucerna autem impiorum extinguetur.
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
Inter superbos semper iurgia sunt: qui autem agunt omnia cum consilio, reguntur sapientia.
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
Substantia festinata minuetur: quae autem paulatim colligitur manu, multiplicabitur.
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
Spes, quae differtur, affligit animam: lignum vitae desiderium veniens.
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
Qui detrahit alicui rei, ipse se in futurum obligat: qui autem timet praeceptum, in pace versabitur. Animae dolosae errant in peccatis: iusti autem misericordes sunt, et miserantur.
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
Lex sapientis fons vitae, ut declinet a ruina mortis.
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
Doctrina bona dabit gratiam: in itinere contemptorum vorago.
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
Astutus omnia agit cum consilio: qui autem fatuus est, aperit stultitiam.
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
Nuncius impii cadet in malum: legatus autem fidelis, sanitas.
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
Egestas, et ignominia ei, qui deserit disciplinam: qui autem acquiescit arguenti, glorificabitur.
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
Desiderium si compleatur, delectat animam: detestantur stulti eos, qui fugiunt mala.
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
Qui cum sapientibus graditur, sapiens erit: amicus stultorum similis efficietur.
21 Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
Peccatores persequitur malum: et iustis retribuentur bona.
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
Bonus reliquit heredes filios, et nepotes: et custoditur iusto substantia peccatoris.
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
Multi cibi in novalibus patrum: et aliis congregantur absque iudicio.
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
Qui parcit virgae, odit filium suum: qui autem diligit illum, instanter erudit.
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.
Iustus comedit, et replet animam suam: venter autem impiorum insaturabilis.