< Miyambo 13 >

1 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
A wise son listens to his father’s instruction, but a scoffer does not sh'ma ·hear obey· rebuke.
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
By the fruit of his lips, a man enjoys good things; but the unfaithful crave violence.
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
He who guards his mouth guards his soul. One who opens wide his lips comes to ruin.
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
The soul of the sluggard desires, and has nothing, but the desire of the diligent shall be fully satisfied.
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
A upright man hates lies, but a wicked man brings shame and disgrace.
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
Righteousness guards the way of integrity, but wickedness overthrows the sinner.
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
There are some who pretend to be rich, yet have nothing. There are some who pretend to be poor, yet have great wealth.
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
The ransom of a man’s life is his riches, but the poor sh'ma ·hear obey· no threats.
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
The light of the upright shines brightly, but the lamp candle of the wicked is snuffed out.
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
Pride only breeds quarrels, but with ones who take advice is wisdom.
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
Wealth gained dishonestly dwindles away, but he who gathers by hand makes it grow.
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
Hope deferred makes the heart sick, but when longing is fulfilled, it is a tree of life.
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
Whoever despises instruction will pay for it, but he who respects a charge will be rewarded.
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
The teaching of the wise is a spring of life, to turn from the snares of death.
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
Good understanding wins chen ·grace·; but the way of the unfaithful is hard.
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
Every prudent man acts from knowledge, but a fool exposes folly.
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
A wicked messenger falls into trouble, but a trustworthy envoy gains healing.
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
Poverty and shame come to him who refuses discipline, but he who heeds correction shall be honored.
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
Longing fulfilled is sweet to the soul, but fools detest turning from evil.
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
One who walks with wise men grows wise, but a companion of fools suffers harm.
21 Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
Misfortune pursues sinners, but prosperity rewards the upright.
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
A good man leaves an inheritance to his children’s children, but the wealth of the sinner is stored for the upright.
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
An abundance of food is in poor people’s fields, but lo'mishpat ·injustice· sweeps it away.
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
One who spares the rod hates his son, but one who 'ahav ·affectionately loves· him is careful to discipline him.
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.
The upright one eats to the satisfying of his soul, but the belly of the wicked goes hungry.

< Miyambo 13 >