< Miyambo 13 >
1 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
A wise son—the instruction of a father, And a scorner—he has not heard rebuke.
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
A man eats good from the fruit of the mouth, And the soul of the treacherous—violence.
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
Whoever is keeping his mouth, is keeping his soul, Whoever is opening wide his lips—ruin to him!
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
The soul of the slothful is desiring, and does not have. And the soul of the diligent is made fat.
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
The righteous hates a false word, And the wicked causes abhorrence, and is confounded.
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
Righteousness keeps him who is perfect in the way, And wickedness overthrows a sin offering.
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
There is [he] who is making himself rich, and has nothing, Who is making himself poor, and wealth [is] abundant.
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
The ransom of a man’s life [are] his riches, And the poor has not heard rebuke.
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
The light of the righteous rejoices, And the lamp of the wicked is extinguished.
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
A vain man causes debate through pride, And wisdom [is] with the counseled.
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
Wealth from vanity becomes little, And whoever is gathering by the hand becomes great.
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
Hope prolonged is making the heart sick, And a tree of life [is] the coming desire.
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
Whoever is despising the word is destroyed for it, And whoever is fearing the command is repaid.
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
The law of the wise [is] a fountain of life, To turn aside from snares of death.
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
Good understanding gives grace, And the way of the treacherous [is] hard.
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
Every prudent one deals with knowledge, And a fool spreads out folly.
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
A wicked messenger falls into evil, And a faithful ambassador is healing.
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
Whoever is refusing instruction—poverty and shame, And whoever is observing reproof is honored.
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
A desire accomplished is sweet to the soul, And an abomination to fools [Is] to turn from evil.
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
Whoever is walking with wise men is wise, And a companion of fools suffers evil.
21 Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
Evil pursues sinners, And good repays the righteous.
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
A good man causes sons’ sons to inherit, And the sinner’s wealth [is] laid up for the righteous.
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
Abundance of food—the tillage of the poor, And substance is consumed without judgment.
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
Whoever is sparing his rod is hating his son, And whoever is loving him has hurried his discipline.
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.
The righteous is eating to the satiety of his soul, And the belly of the wicked lacks!