< Miyambo 13 >
1 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
A wise son is instructed of his father; but a scorner heareth not rebuke.
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
A man shall eat good from the fruit of his mouth; but the desire of the faithless is violence.
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
He that guardeth his mouth keepeth his life; but for him that openeth wide his lips there shall be ruin.
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
The soul of the sluggard desireth, and hath nothing; but the soul of the diligent shall be abundantly gratified.
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
A righteous man hateth lying; but a wicked man behaveth vilely and shamefully.
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
Righteousness guardeth him that is upright in the way; but wickedness overthroweth the sinner.
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
There is that pretendeth himself rich, yet hath nothing; there is that pretendeth himself poor, yet hath great wealth.
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
The ransom of a man's life are his riches; but the poor heareth no threatening.
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
The light of the righteous rejoiceth; but the lamp of the wicked shall be put out.
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
By pride cometh only contention; but with the well-advised is wisdom.
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
Wealth gotten by vanity shall be diminished; but he that gathereth little by little shall increase.
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
Hope deferred maketh the heart sick; but desire fulfilled is a tree of life.
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
Whoso despiseth the word shall suffer thereby; but he that feareth the commandment shall be rewarded.
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
The teaching of the wise is a fountain of life, to depart from the snares of death.
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
Good understanding giveth grace; but the way of the faithless is harsh.
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
Every prudent man dealeth with forethought; but a fool unfoldeth folly.
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
A wicked messenger falleth into evil; but a faithful ambassador is health.
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
Poverty and shame shall be to him that refuseth instruction; but he that regardeth reproof shall be honoured.
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
The desire accomplished is sweet to the soul; and it is an abomination to fools to depart from evil.
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
He that walketh with wise men shall be wise; but the companion of fools shall smart for it.
21 Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
Evil pursueth sinners; but to the righteous good shall be repaid.
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
A good man leaveth an inheritance to his children's children; and the wealth of the sinner is laid up for the righteous.
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
Much food is in the tillage of the poor; but there is that is swept away by want of righteousness.
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
He that spareth his rod hateth his son; but he that loveth him chasteneth him betimes.
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.
The righteous eateth to the satisfying of his desire; but the belly of the wicked shall want.