< Miyambo 13 >

1 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
A wise son accepts his father's discipline, but a mocker doesn't listen to correction.
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
You'll be rewarded for saying good things, but dishonest people want violence.
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
Watch what you say and save your life—saying too much leads to disaster.
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
Lazy people want a lot, but get nothing; if you work hard you'll be well rewarded.
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
Good people hate lies, but the wicked cause a stink and bring disgrace.
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
Goodness protects those who live right, but sin overcomes the wicked.
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
Some pretend to be rich, but don't have anything, while others pretend to be poor and are very rich.
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
The rich can pay a ransom to save their lives, but the poor aren't troubled in this way.
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
The life of good people shines brightly, but the lamp of the wicked will be snuffed out.
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
Pride only causes conflict; but those who take advice are wise.
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
Wealth gained by fraud quickly disappears, but those who gather bit by bit prosper.
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
Hope that's delayed makes you feel sick, but a wish that comes true revives you.
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
If you despise words of advice, you'll pay for it; but if you respect what you're told, you'll be rewarded.
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
The teaching of the wise is like a fountain of life, so you can avoid the snares of death.
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
Good sense earns appreciation, but the way of the unfaithful is hard.
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
All wise people act intelligently, but stupid people demonstrate their stupidity.
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
A bad messenger creates trouble, but a faithful representative brings healing.
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
Poverty and disgrace come to those who ignore instruction, but those who accept correction are honored.
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
It's nice to see a wish come true, but stupid people hate to turn away from evil to achieve this.
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
Being friends with wise people will make you wise, but being friends with stupid people will only cause you problems.
21 Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
Tragedy chases after the sinner, but prosperity rewards the good.
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
Good people leave an inheritance to their grandchildren, but the sinner's wealth is saved for those who live right.
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
The unploughed ground of the poor could produce a lot of food, but it's stolen through injustice.
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
People who don't discipline their children hate them. Those who love their children carefully discipline them.
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.
The good eat until they're full; but the belly of the wicked is empty.

< Miyambo 13 >