< Miyambo 13 >

1 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
智慧之子,聽從父親的教訓;輕狂的人,不聽任何人規勸。
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
義人必飽嘗自己口舌的果實,惡人的慾望只有飽食強暴。
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
謹口慎言,方能自保性命;信口開河,終必自取滅亡。
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
懶人雖常盼望,卻一無所得;勤勞的人,卻常如願以償。
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
義人憎惡謊言,惡人令人可憎可惡。
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
正義保衛行為正直的人,邪惡卻使罪人滅亡。
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
有人自充富人,其實一貧如洗;有人佯作窮人,其實腰纏萬貫。
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
富人的錢財只是性命的贖價,窮人卻沒有這樣的威脅。
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
義人的光明,必要高升;惡人的燈火,勢必熄滅。
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
傲慢只有引起爭端,虛心受教的人纔有智慧。
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
儻來之物,容易消逝;經久積存,日漸增多。
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
希望遲不兌現,令人心神煩惱;願望獲得滿足,像株生命樹。
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
誰輕視法令,必遭滅亡;誰敬畏誡命,必得安全。
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
智慧人的教訓是生命的泉源,人可賴以脫免死亡的羅網。
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
明哲的規勸,使人蒙恩,殘暴人的舉止,粗魯蠻橫。
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
精明的人,常按理智行事;愚昧的人,只自誇其糊塗。
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
奸妄的使者,使人陷於災禍;忠誠的使者,給人帶來安和。
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
拒絕規勸的,必遭貧苦羞辱;接受懲戒的,反要受人尊敬。
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
願望獲得滿足,能使心靈愉快;遠離邪惡,卻為愚昧人所深惡。
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
與智慧人往來,可成智慧人;與愚昧人作伴,必受其連累。
21 Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
惡運追蹤罪人,義人卻得善報。
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
善人為子子孫孫留下產業,罪人的財富是為義人積蓄。
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
窮人開墾的田地,生產大量食物;誰若缺乏正義,定不免於滅亡。
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
不肯使用棍杖的人,實是恨自己的兒子;真愛兒子的人,必時加以懲罰。
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.
義人必得飽食,惡人無以果腹。

< Miyambo 13 >