< Miyambo 12 >

1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
Den som älskar tuktan, han älskar kunskap, men oförnuftig är den som hatar tillrättavisning.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
Den gode undfår nåd av HERREN, men den ränkfulle varder av honom fördömd.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
Ingen människa bliver beståndande genom ogudaktighet, men de rättfärdigas rot kan icke rubbas.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
En idog hustru är sin mans krona, men en vanartig är såsom röta i hans ben.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
De rättfärdigas tankar gå ut på vad rätt är, men de ogudaktigas rådklokhet går ut på svek.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
De ogudaktigas ord ligga på lur efter blod, men de redliga räddas genom sin mun.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
De ogudaktiga varda omstörtade och äro så icke mer, men de rättfärdigas hus består.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
I mån av sitt vett varder en man prisad, men den som har ett förvänt förstånd, han bliver föraktad.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Bättre är en ringa man, som likväl har en tjänare, än den som vill vara förnäm och saknar bröd.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
Den rättfärdige vet huru hans boskap känner det, men de ogudaktigas hjärtelag är grymt.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
Den som brukar sin åker får bröd till fyllest, men oförståndig är den som far efter fåfängliga ting.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
Den ogudaktige vill in i det nät som fångar de onda, men de rättfärdigas rot skjuter skott.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
Den som är ond bliver snärjd i sina läppars synd, men den rättfärdige undkommer ur nöden
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
Sin muns frukt får envar njuta sig fullt till godo, och vad en människas händer hava förövat, det varder henne vedergällt.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
Den oförnuftige tycker sin egen väg vara den rätta, med den som är vis lyssnar till råd.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
Den oförnuftiges förtörnelse bliver kunnig samma dag, men den som är klok, han döljer sin skam
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
Den som talar vad rätt är, han främjar sanning, men ett falskt vittne talar svek.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
Mången talar i obetänksamhet ord som stinga likasom svärd, men de visas tunga är en läkedom.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
Sannfärdiga läppar bestå evinnerligen, men en lögnaktig tunga allenast ett ögonblick.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
De som bringa ont å bane hava falskhet i hjärtat, men de som stifta frid, de undfå glädje.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
Intet ont vederfares den rättfärdige, men över de ogudaktiga kommer olycka i fullt mått.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
En styggelse för HERREN äro lögnaktiga låppar, men de som handla redligt behaga honom väl.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
En klok man döljer sin kunskap, men dårars hjärtan ropa ut sitt oförnuft.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
De idogas hand kommer till välde, men en lat hand måste göra trältjänst.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
Sorg i en mans hjärta trycker det ned, men ett vänligt ord skaffar det glädje.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
Den rättfärdige visar sin vän till rätta, men de ogudaktigas väg för dem själva vilse.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
Den late får icke upp något villebråd, men idoghet är för människan en dyrbar skatt.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
På rättfärdighetens väg är liv, och där dess stig går fram är frihet ifrån död.

< Miyambo 12 >