< Miyambo 12 >

1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
El que ama la corrección ama el conocimiento, Pero el que aborrece la reprensión es estúpido.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
El bueno obtendrá el favor de Yavé, Pero Él condenará al hombre de malos designios.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
El hombre no se afianzará por medio de la perversidad, Pero la raíz de los justos nunca será removida.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
La mujer virtuosa es corona de su esposo, Pero la que lo avergüenza es como carcoma en sus huesos.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
Los pensamientos de los justos son rectos, Pero los consejos de los impíos, engaño.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
Las palabras de los perversos son asechanzas mortales, Pero la boca de los rectos los librará.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
Se derrumban los perversos y ya no existen, Pero la casa de los justos permanecerá.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
Según su sabiduría es alabado el hombre, Pero el perverso de corazón será despreciado.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Mejor es el poco estimado, Pero que tiene un esclavo, Que el que se alaba y carece de pan.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
El justo tiene en consideración la vida de su bestia, Pero aun la compasión de los perversos es cruel.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
El que labra su tierra, se saciará de pan, Pero el que persigue lo vano carece de entendimiento.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
El perverso codicia el botín de los perversos, Pero la raíz de los justos produce.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
En la transgresión de sus labios se enreda el perverso, Pero el justo escapará de la aflicción.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
De lo que uno habla, se saciará, Y por lo que uno hace, le pagarán.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
El camino del necio es recto ante sus propios ojos, Pero el que escucha el consejo es sabio.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
La ira del necio es conocida al instante, Pero el prudente pasa por alto la ofensa.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
El testigo veraz declara lo que es recto, Pero el testigo falso engaña.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
Hay quien pronuncia palabras como estocadas, Pero la boca de los sabios es medicina.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
El labio veraz permanece para siempre, Pero la boca mentirosa, solo un instante.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
Hay engaño en el corazón del que trama el mal, Pero para los consejeros de la paz hay alegría.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
Ninguna iniquidad es deseada por el justo, Pero los perversos están llenos de mal.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
Repugnancia es a Yavé el labio mentiroso, Pero su deleite está en los que obran fielmente.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
El hombre prudente encubre su conocimiento, Pero el corazón de los necios proclama su necedad.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
La mano del diligente señoreará, Pero la indolente será tributaria.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
La congoja abate el corazón del hombre, Pero la buena palabra lo alegra.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
El justo sirve de guía a su prójimo, Pero el camino de los perversos los hace errar.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
El indolente no asará ni su propia presa. ¡Precioso tesoro del hombre es la diligencia!
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
En la senda de la justicia está la vida, En su sendero no hay muerte.

< Miyambo 12 >