< Miyambo 12 >

1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
Kdorkoli ljubi poučevanje, ljubi spoznanje, toda kdor sovraži opomin, je brutalen.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
Dober človek doseže naklonjenost od Gospoda, toda človek zlobnih naklepov bo obsojen.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
Človek ne bo uveljavljen z zlobnostjo, toda korenina pravičnih ne bo omajana.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
Vrla ženska je krona svojemu soprogu, toda tista, ki sramoti, je gniloba v njegovih kosteh.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
Misli pravičnih so pravilne, toda nasveti zlobnih so prevara.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
Besede zlobnih so prežanje v zasedi na kri, toda usta iskrenih jih bodo osvobodila.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
Zlobni so premagani in jih ni, toda hiša pravičnega bo stala.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
Človek bo priporočen glede na svojo modrost, toda kdor je sprevrženega srca, bo preziran.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Kdor je preziran, pa ima služabnika, je boljši kakor tisti, ki časti samega sebe, pa nima kruha.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
Pravičen človek se ozira na življenje svoje živali, toda nežna usmiljenja zlobnih so kruta.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
Kdor obdeluje svojo zemljo, bo nasičen s kruhom, toda kdor sledi praznim osebam, je brez razumevanja.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
Zlobni želi mrežo zlobnih ljudi, toda korenina pravičnih rojeva sad.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
Zlobni je ujet s prestopkom svojih ustnic, toda pravični bo prišel iz stiske.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
Človek bo nasičen z dobrim po sadu svojih ust in poplačilo človeških rok mu bo vrnjeno.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
Bedakova pot je v njegovih lastnih očeh pravilna, toda kdor prisluhne nasvetu, je moder.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
Bedakov bes je takoj znan, toda razsoden človek prikriva sramoto.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
Kdor govori resnico, naznanja pravičnost, toda kriva priča prevaro.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
Tam je, ki govori kakor prebadanje z mečem, toda jezik modrega je zdravje.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
Ustnica resnice bo utrjena za vedno, toda lažniv jezik je samo za trenutek.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
Prevara je v srcu tistih, ki si domišljajo zlo, toda svetovalcem miru je radost.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
Nobeno zlo se ne bo zgodilo pravičnemu, toda zlobni bodo napolnjeni z vragolijo.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
Lažnive ustnice so ogabnost Gospodu, toda tisti, ki se vedejo odkrito, so njegovo veselje.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
Razsoden človek prikriva spoznanje, toda srce bedakov razglaša nespametnost.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
Roka marljivega bo vladala, toda leni bo podvržen plačevanju davka.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
Potrtost v človekovem srcu ga dela sklonjenega, toda dobra beseda ga dela veselega.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
Pravični je odličnejši od svojega soseda, toda pot zlobnih jih zapeljuje.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
Len človek ne peče tega, kar je ujel na lovu, toda imetje marljivega človeka je dragoceno.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
Na poti pravičnosti je življenje in na tej poti ni smrti.

< Miyambo 12 >