< Miyambo 12 >
1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
Ко љуби наставу, љуби знање; а ко мрзи на укор, остаје луд.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
Добар човек добија љубав од Господа, а човека зликовца осуђује.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
Неће се човек утврдити безбожношћу, а корен праведних неће се помаћи.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
Вредна је жена венац мужу свом; а која га срамоти, она му је као трулеж у костима.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
Мисли су праведних праве, а савети безбожних превара.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
Речи безбожних вребају крв, а праведне избављају уста њихова.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
Обарају се безбожни да их нема, а дом праведних остаје.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
Према разуму свом хвали се човек; а ко је опака срца, презреће се.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Ко се снебива, а има слугу, бољи је од оног који се велича а хлеба нема.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
Праведник се брине за живот свог живинчета, а у безбожника је срце немилостиво.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
Ко ради своју земљу, биће сит хлеба; а ко иде за беспослицама, безуман је.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
Безбожник жели обрану ода зла, али корен праведних даје је.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
Зломе је замка у греху усана његових, а праведник излази из тескобе.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
Од плода уста својих сити се човек добра, и плату за дела своја прима човек.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
Безумнику се чини прав пут његов; али ко слуша савет, мудар је.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
Гнев безумников одмах се позна, али паметни покрива срамоту.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
Ко говори истину, јавља шта је право, а лажни сведок превару.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
Има ко говори као да мач пробада, а језик је мудрих лек.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
Истинита уста стоје тврдо довека, а језик лажљиви за час.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
Који зло мисле, превара им је у срцу, а радост је онима који саветују на мир.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
Никаква несрећа неће задесити праведника, а безбожници ће се напунити зла.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
Мрске су Господу лажљиве усне; а који раде верно, мили су Му.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
Паметан човек покрива знање, а срце безумних разглашује безумље.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
Рука радљива господариће, а лена ће давати данак.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
Брига у срцу човечијем обара; а добра реч развесељава.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
Праведнику је боље него ближњему његовом; а безбожнике заводи пут њихов.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
Лењивац неће пећи лов свој, а у вредног је човека добро драгоцено.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
На путу правде живот је, и куда иде стаза њена нема смрти.