< Miyambo 12 >
1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
O que ama a correcção ama o conhecimento, mas o que aborrece a reprehensão é brutal.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
O homem de bem alcançará o favor do Senhor, mas ao homem de perversas imaginações elle condemnará.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
O homem não se estabelecerá pela impiedade, mas a raiz dos justos não será removida.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
A mulher virtuosa é a corôa do seu senhor, mas a que faz vergonha é como apodrecimento nos seus ossos.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
Os pensamentos dos justos são juizo, mas os conselhos dos impios engano.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
As palavras dos impios são de armarem ciladas ao sangue, mas a bocca dos rectos os fará escapar.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
Transtornados serão os impios, e não serão mais, mas a casa dos justos permanecerá.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
Segundo o seu entendimento, será louvado cada qual, mas o perverso de coração estará em desprezo.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Melhor é o que se estima em pouco, e tem servos, do que o que se honra a si mesmo e tem falta de pão.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
O justo attende pela vida dos seus animaes, mas as misericordias dos impios são crueis.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
O que lavra a sua terra se fartará de pão mas o que segue os ociosos está falto de juizo.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
Deseja o impio a rede dos males, mas a raiz dos justos produz o seu fructo.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
O laço do impio está na transgressão dos labios, mas o justo sairá da angustia.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
Do fructo da bocca cada um se farta de bem, e a recompensa das mãos dos homens se lhe tornará.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
O caminho do tolo é recto aos seus olhos, mas o que dá ouvidos ao conselho é sabio.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
A ira do louco se conhece no mesmo dia, mas o avisado encobre a affronta.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
O que produz a verdade manifesta a justiça, mas a testemunha da falsidade o engano.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
Ha alguns que fallam palavras como estocadas de espada, mas a lingua dos sabios é saude.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
O labio de verdade ficará para sempre, mas a lingua de falsidade dura por um só momento.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
Engano ha no coração dos que maquinam mal, mas alegria teem os que aconselham a paz.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
Nenhum aggravo sobrevirá ao justo, mas os impios ficam cheios de mal.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
Os labios mentirosos são abominaveis ao Senhor, mas os que obram fielmente são o seu deleite.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
O homem avisado encobre o conhecimento, mas o coração dos tolos proclama a estulticia.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
A mão dos diligentes dominará, mas os enganadores serão tributarios.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
A solicitude no coração do homem o abate, mas uma boa palavra o alegra.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
Mais excellente é o justo do que o companheiro, mas o caminho dos impios os faz errar.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
O preguiçoso não assará a sua caça, mas o precioso bem do homem é ser diligente.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
Na vereda da justiça está a vida, e no caminho da sua carreira não ha morte.