< Miyambo 12 >
1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
訓誨を愛する者は知識を愛す 懲戒を惡むものは畜のごとし
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
善人はヱホバの恩寵をうけ 惡き謀略を設くる人はヱホバに罰せらる
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
人は惡をもて堅く立ことあたはず 義人の根は動くことなし
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
賢き婦はその夫の冠弁なり 辱をきたらする婦は夫をしてその骨に腐あるが如くならしむ
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
義者のおもひは直し 惡者の計るところは虚偽なり
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
惡者の言は人の血を流さんとて伺ふ されど直者の口は人を救ふなり
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
惡者はたふされて無ものとならん されど義者の家は立べし
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
人はその聰明にしたがひて譽られ 心の悖れる者は藐めらる
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
卑賤してしもべある者は自らたかぶりて食に乏き者に愈る
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
義者はその畜の生命を顧みる されど惡者は殘忍をもてその憐憫とす
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
おのれの田地を耕すものは食にあく 放蕩なる人にしたがふ者は智慧なし
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
惡者はあしき人の獲たる物をうらやみ 義者の根は芽をいだす
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
惡者はくちびるの愆によりて罟に陷る されど義者は患難の中よりまぬかれいでん
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
人はその口の徳によりて福祉に飽ん 人の手の行爲はその人の身にかへるべし
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
愚なる者はみづからその道を見て正しとす されど智慧ある者はすすめを容る
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
愚なる者はただちに怒をあらはし 智きものは恥をつつむ
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
眞實をいふものは正義を述べ いつはりの證人は虚偽をいふ
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
妄りに言をいだし劍をもて刺がごとくする者あり されど智慧ある者の舌は人をいやす
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
眞理をいふ口唇は何時までも存つ されど虚偽をいふ舌はただ瞬息のあひだのみなり
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
惡事をはかる者の心には欺詐あり 和平を謀る者には歓喜あり
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
義者には何の禍害も來らず 惡者はわざはひをもて充さる
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
いつはりの口唇はヱホバに憎まれ 眞實をおこなふ者は彼に悦ばる
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
賢人は知識をかくす されど愚なる者のこころは愚なる事を述ぶ
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
勤めはたらく者の手は人ををさむるにいたり惰者は人に服ふるにいたる
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
うれひ人の心にあれば之を屈ます されど善言はこれを樂します
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
義者はその友に道を示す されど惡者は自ら途にまよふ
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
惰者はおのれの猟獲たる物をも燔ず 勉めはたらくことは人の貴とき寳なり
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
義しき道には生命ありその道すぢには死なし