< Miyambo 12 >
1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
Celui qui aime la discipline aime la science: mais celui qui hait les réprimandes est insensé.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
Celui qui est bon puisera la grâce dans le Seigneur; mais celui qui se confie dans ses pensées agit en impie.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
L’homme ne s’affermira point par l’impiété: et la racine des justes ne sera pas ébranlée.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
Une femme diligente est une couronne pour son mari: et c’est la carie dans les os du sien qu’une femme qui fait des choses dignes de confusion.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
Les pensées des justes sont des jugements; les conseils des impies sont frauduleux.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
Les paroles des impies dressent des embûches au sang; la bouche des justes les délivrera.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
Renversez les impies, ils ne seront plus; mais la maison du juste demeurera à jamais.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
C’est par sa doctrine que sera connu un homme; mais celui qui est vain et sans cœur sera ouvert au mépris.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Mieux vaut un pauvre se suffisant à lui-même, qu’un glorieux qui manque de pain.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
Le juste connaît les âmes de ses bêtes; mais les entrailles des impies sont cruelles.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
Celui qui travaille sa terre sera rassasié de pain; mais celui qui cherche l’oisiveté est très insensé. Celui à qui il est doux de passer le temps à boire du vin laisse dans ses fortifications du déshonneur.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
Le désir d’un impie est l’appui des plus méchants; mais la racine des justes prospérera.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
À cause du péché de ses lèvres, la ruine s’approche du méchant; mais le juste échappera à l’angoisse.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
En vertu du fruit de sa bouche, chacun sera rempli de biens, et selon les œuvres de ses mains il lui sera rendu.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
La voie d’un insensé est droite à ses yeux; mais celui qui est sage écoute les conseils.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
L’insensé découvre soudain sa colère: mais celui qui dissimule une injure est habile.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
Celui qui dit ce qu’il sait rend un témoignage juste; mais celui qui ment est un témoin frauduleux.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
Il est tel qui promet et qui ensuite est percé comme du glaive de sa conscience; mais la langue des sages est la santé.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
La lèvre véridique sera ferme à perpétuité; mais celui qui est témoin précipité se fait une langue de mensonge.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
La fraude est dans le cœur de ceux qui pensent des choses mauvaises; mais ceux qui entrent dans des conseils de paix, la joie les suit.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
Rien ne contristera le juste, quoi qu’il lui arrive: mais les impies seront remplis de maux.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
C’est une abomination pour le Seigneur, que des lèvres menteuses; mais ceux qui sincèrement agissent lui plaisent.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
Un homme habile cache sa science; et le cœur des insensés publie leur folie.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
La main des forts dominera; mais celle qui est relâchée sera soumise aux tributs.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
La tristesse dans le cœur d’un homme l’humiliera; et par une bonne parole il sera réjoui.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
Celui qui néglige un dommage à cause d’un ami est juste; mais le chemin des impies les trompera.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
Le frauduleux ne trouvera pas de gain; et la richesse d’un homme juste sera d’un prix d’or.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
Dans le sentier de la justice est la vie; mais le chemin détourné conduit à la mort.