< Miyambo 12 >
1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
Celui qui aime la correction aime la science; Celui qui hait la réprimande est stupide.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
L’homme de bien obtient la faveur de l’Éternel, Mais l’Éternel condamne celui qui est plein de malice.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
L’homme ne s’affermit pas par la méchanceté, Mais la racine des justes ne sera point ébranlée.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
Une femme vertueuse est la couronne de son mari, Mais celle qui fait honte est comme la carie dans ses os.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
Les pensées des justes ne sont qu’équité; Les desseins des méchants ne sont que fraude.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
Les paroles des méchants sont des embûches pour verser le sang, Mais la bouche des hommes droits est une délivrance.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
Renversés, les méchants ne sont plus; Et la maison des justes reste debout.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
Un homme est estimé en raison de son intelligence, Et celui qui a le cœur pervers est l’objet du mépris.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Mieux vaut être d’une condition humble et avoir un serviteur Que de faire le glorieux et de manquer de pain.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
Le juste prend soin de son bétail, Mais les entrailles des méchants sont cruelles.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
Celui qui cultive son champ est rassasié de pain, Mais celui qui poursuit des choses vaines est dépourvu de sens.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
Le méchant convoite ce que prennent les méchants, Mais la racine des justes donne du fruit.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
Il y a dans le péché des lèvres un piège pernicieux, Mais le juste se tire de la détresse.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
Par le fruit de la bouche on est rassasié de biens, Et chacun reçoit selon l’œuvre de ses mains.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
La voie de l’insensé est droite à ses yeux, Mais celui qui écoute les conseils est sage.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
L’insensé laisse voir à l’instant sa colère, Mais celui qui cache un outrage est un homme prudent.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
Celui qui dit la vérité proclame la justice, Et le faux témoin la tromperie.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
Tel, qui parle légèrement, blesse comme un glaive; Mais la langue des sages apporte la guérison.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
La lèvre véridique est affermie pour toujours, Mais la langue fausse ne subsiste qu’un instant.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
La tromperie est dans le cœur de ceux qui méditent le mal, Mais la joie est pour ceux qui conseillent la paix.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
Aucun malheur n’arrive au juste, Mais les méchants sont accablés de maux.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
Les lèvres fausses sont en horreur à l’Éternel, Mais ceux qui agissent avec vérité lui sont agréables.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
L’homme prudent cache sa science, Mais le cœur des insensés proclame la folie.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
La main des diligents dominera, Mais la main lâche sera tributaire.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
L’inquiétude dans le cœur de l’homme l’abat, Mais une bonne parole le réjouit.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
Le juste montre à son ami la bonne voie, Mais la voie des méchants les égare.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
Le paresseux ne rôtit pas son gibier; Mais le précieux trésor d’un homme, c’est l’activité.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
La vie est dans le sentier de la justice, La mort n’est pas dans le chemin qu’elle trace.