< Miyambo 12 >

1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
Qui aime la réprimande aime la science; mais qui hait les remontrances est un sot.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
L’Homme bon s’attire la bienveillance de l’Eternel, l’homme artificieux sa réprobation:
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
On ne se maintient pas par l’iniquité; mais les justes jettent des racines inébranlables.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
Une femme vertueuse est la couronne de son époux; une dévergondée, c’est la carie dans ses os.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
Les justes ne rêvent que justice, les méchants ne combinent que tromperies.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
Les méchants ne parlent que de dresser des embûches meurtrières; mais la bouche des justes ne s’applique qu’à sauver.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
Une secousse, et les méchants ne sont plus! Mais la demeure des justes est stable.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
En proportion de son intelligence, l’homme mérite des éloges; mais les cœurs obliques sont un objet de mépris.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Mieux vaut être dédaigné et posséder un esclave, que de faire le grand et manquer de pain.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
Le juste a le souci du bien-être de ses bêtes; mais les entrailles des méchants ne connaissent pas la pitié.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
Celui qui cultive sa terre a du pain à satiété; celui qui poursuit des frivolités manque de sens.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
L’Impie convoite ce qui devient un piège pour les méchants; mais la racine des justes est généreuse en fruits.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
Les lèvres criminelles constituent un piège funeste; mais le juste échappe à la peine.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
L’Homme doit à l’usage de la parole le bien dont il jouit; on paie à chacun le prix de ses œuvres.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
La voie de l’insensé paraît droite à ses yeux; mais écouter des conseils, c’est être sage.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
Le sot, sur l’heure, manifeste son dépit; un habile homme sait dévorer un affront.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
Celui qui est épris de loyauté expose fidèlement les faits; le témoin mensonger les dénature.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
Il en est dont la parole blesse comme des coups d’épée, mais, le langage des sages est un baume bienfaisant.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
La vérité est éternelle; le mensonge dure un clin d’œil.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
Dans le cœur de ceux qui méditent le mal s’il n’y a que perfidie; chez ceux qui donnent des conseils salutaires, il n’y a que joie.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
Aucune calamité ne surprend le juste; mais les méchants sont accablés de maux.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
L’Eternel a horreur des lèvres mensongères; mais il aime ceux qui agissent avec loyauté.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
Un homme avisé ne fait pas montre de son savoir; les esprits sots crient leur sottise.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
La main diligente assure le pouvoir; la main négligente paie tribut.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
Le souci abat le cœur de l’homme; mais une bonne parole y ramène la joie.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
Supérieur à tous est le juste; les méchants suivent un chemin qui les égare.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
La paresse évite de mettre son gibier sur le feu; mais l’activité est un trésor précieux pour l’homme.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
Sur le chemin de la vertu se trouve la vie, et son sentier aboutit à l’immortalité.

< Miyambo 12 >