< Miyambo 12 >

1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
Qui aime l’instruction aime la connaissance, et qui hait la répréhension est stupide.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
L’homme de bien obtient la faveur de par l’Éternel, mais l’homme qui fait des machinations, il le condamne.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
L’homme n’est point affermi par la méchanceté, mais la racine des justes n’est pas ébranlée.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
Une femme vertueuse est la couronne de son mari, mais celle qui fait honte est comme de la pourriture dans ses os.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
Les pensées des justes sont jugement, les desseins des méchants sont fraude.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
Les paroles des méchants sont des embûches pour [verser] le sang, mais la bouche des hommes droits les délivrera.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
Renversez les méchants, et ils ne sont plus; mais la maison des justes demeure.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
Un homme est loué d’après sa prudence, mais le cœur perverti est en butte au mépris.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Mieux vaut celui qui est d’humble condition, et qui a un serviteur, que celui qui fait l’important et qui manque de pain.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
Le juste regarde à la vie de sa bête, mais les entrailles des méchants sont cruelles.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
Celui qui laboure sa terre sera rassasié de pain, mais celui qui court après les fainéants est dépourvu de sens.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
Le méchant désire la proie des mauvaises gens, mais la racine des justes est productive.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
Il y a un mauvais piège dans la transgression des lèvres, mais le juste sort de la détresse.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
Du fruit de sa bouche un homme est rassasié de biens, et on rendra à l’homme l’œuvre de ses mains.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
La voie du fou est droite à ses yeux, mais celui qui écoute le conseil est sage.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
L’irritation du fou se connaît le jour même, mais l’homme avisé couvre sa honte.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
Celui qui dit la vérité annonce la justice, mais le faux témoin, la fraude.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
Il y a tel homme qui dit légèrement ce qui perce comme une épée, mais la langue des sages est santé.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
La lèvre véridique est ferme pour toujours, mais la langue fausse n’est que pour un instant.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
La fraude est dans le cœur de ceux qui machinent le mal, mais il y a de la joie pour ceux qui conseillent la paix.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
Aucun malheur n’arrive au juste, mais les méchants seront comblés de maux.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
Les lèvres menteuses sont en abomination à l’Éternel, mais ceux qui pratiquent la fidélité lui sont agréables.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
L’homme avisé couvre la connaissance, mais le cœur des sots proclame la folie.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
La main des diligents dominera, mais la [main] paresseuse sera tributaire.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
L’inquiétude dans le cœur d’un homme l’abat, mais une bonne parole le réjouit.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
Le juste montre le chemin à son compagnon, mais la voie des méchants les fourvoie.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
Le paresseux ne rôtit pas sa chasse; mais les biens précieux de l’homme sont au diligent.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
La vie est dans le sentier de la justice, et il n’y a pas de mort dans le chemin qu’elle trace.

< Miyambo 12 >