< Miyambo 12 >

1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
Whoever loves correction loves knowledge, but he who hates reproof is stupid.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
A good man shall obtain favor from the LORD, but he will condemn a man of wicked devices.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
A man shall not be established by wickedness, but the root of the righteous shall not be moved.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
A worthy woman is the crown of her husband, but a disgraceful wife is as rottenness in his bones.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
The thoughts of the righteous are just, but the advice of the wicked is deceitful.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
The words of the wicked are about lying in wait for blood, but the speech of the upright rescues them.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
The wicked are overthrown, and are no more, but the house of the righteous shall stand.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
A person is commended according to his good sense, but the one who has a perverse mind is despised.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Better is he who is lightly esteemed, and has a servant, than he who honors himself, and lacks bread.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
A righteous man regards the life of his animal, but the tender mercies of the wicked are cruel.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
He who tills his land shall have plenty of bread, but he who chases fantasies is void of understanding.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
The wicked desires the plunder of evil men, but the root of the righteous flourishes.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
An evil man is trapped by sinfulness of lips, but the righteous shall come out of trouble.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
A man shall be satisfied with good by the fruit of his mouth. The work of a man's hands shall be rewarded to him.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
The way of a fool is right in his own eyes, but he who is wise listens to counsel.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
A fool shows his annoyance the same day, but one who overlooks an insult is prudent.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
He who is truthful testifies honestly, but a false witness lies.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
There is one who speaks rashly like the piercing of a sword, but the tongue of the wise heals.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
Truth's lips will be established forever, but a lying tongue is only momentary.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
Deceit is in the heart of those who plot evil, but joy comes to the promoters of peace.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
No mischief shall happen to the righteous, but the wicked shall be filled with evil.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
Lying lips are an abomination to the LORD, but those who do the truth are his delight.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
A prudent man keeps his knowledge, but the hearts of fools proclaim foolishness.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
The hands of the diligent ones shall rule, but laziness ends in slave labor.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
Anxiety in a man's heart weighs it down, but a kind word makes it glad.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
A righteous person is cautious in friendship, but the way of the wicked leads them astray.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
The slothful man doesn't roast his game, but the possessions of diligent men are prized.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
In the way of righteousness is life; in its path there is no death.

< Miyambo 12 >