< Miyambo 12 >

1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
Whoever is loving instruction, is loving knowledge, And whoever is hating reproof [is] brutish.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
The good brings forth favor from YHWH, And the man of wicked schemes He condemns.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
A man is not established by wickedness, And the root of the righteous is not moved.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
A virtuous woman [is] a crown to her husband, And as rottenness in his bones [is] one causing shame.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
The thoughts of the righteous [are] justice, The counsels of the wicked—deceit.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
The words of the wicked [are]: “Lay [in] wait for blood,” And the mouth of the upright delivers them.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
Overthrow the wicked, and they are not, And the house of the righteous stands.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
A man is praised according to his wisdom, And the perverted of heart becomes despised.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Better [is] the lightly esteemed who has a servant, Than the self-honored who lacks bread.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
The righteous knows the life of his beast, And the mercies of the wicked [are] cruel.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
Whoever is tilling the ground is satisfied [with] bread, And whoever is pursuing vanities is lacking heart,
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
The wicked has desired the net of evildoers, And the root of the righteous gives.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
The snare of the wicked [is] in transgression of the lips, And the righteous goes out from distress.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
One [is] satisfied [with] good from the fruit of the mouth, And the deed of man’s hands returns to him.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
The way of a fool [is] right in his own eyes, And whoever is listening to counsel [is] wise.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
The fool—his anger is known in a day, And the prudent is covering shame.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
Whoever utters faithfulness declares righteousness, And a false witness—deceit.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
A rash speaker is like piercings of a sword, And the tongue of the wise is healing.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
The lip of truth is established forever, And a tongue of falsehood for a moment.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
Deceit [is] in the heart of those devising evil, But for counselors of peace—joy.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
No iniquity is desired by the righteous, And the wicked have been full of evil.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
Lying lips [are] an abomination to YHWH, And steadfast doers [are] his delight.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
A prudent man is concealing knowledge, And the heart of fools proclaims folly.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
The hand of the diligent rules, And slothfulness becomes tributary.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
Sorrow in the heart of a man bows down, And a good word makes him glad.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
The righteous searches his companion, And the way of the wicked causes them to err.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
The slothful does not roast his game, And the wealth of a diligent man is precious.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
In the path of righteousness [is] life, And in the way of [that] path [is] no death!

< Miyambo 12 >