< Miyambo 12 >
1 Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
At elske Tugt er at elske Kundskab, at hade Revselse er dumt.
2 Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
Den gode vinder Yndest hos HERREN, den rænkefulde dømmer han skyldig.
3 Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
Ingen staar fast ved Gudløshed, men retfærdiges Rod skal aldrig rokkes.
4 Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
En duelig Kvinde er sin Ægtemands Krone, en daarlig er som Edder i hans Ben.
5 Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
Retfærdiges Tanker er Ret, gudløses Opspind er Svig.
6 Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
Gudløses Ord er paa Lur efter Blod, retsindiges Mund skal bringe dem Frelse.
7 Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
Gudløse styrtes og er ikke mer, retfærdiges Hus staar fast.
8 Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
For sin Klogskab prises en Mand, til Spot bliver den, hvis Vid er vrangt.
9 Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
Hellere overses, naar man holder Træl, end optræde stort, naar man mangler Brød.
10 Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
Den retfærdige føler med sit Kvæg, gudløses Hjerte er grumt.
11 Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
Den mættes med Brød, som dyrker sin Jord, uden Vid er den, der jager efter Tomhed.
12 Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
De ondes Fæstning jævnes med Jorden, de retfærdiges Rod holder Stand.
13 Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
I Læbernes Brøde hildes den onde, den retfærdige undslipper Nøden.
14 Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
Af sin Munds Frugt mættes en Mand med godt, et Menneske faar, som hans Hænder har øvet.
15 Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
Daarens Færd behager ham selv, den vise hører paa Raad.
16 Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
En Daare giver straks sin Krænkelse Luft, den kloge spottes og lader som intet.
17 Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
Den sanddru fremfører, hvad der er ret, det falske Vidne kommer med Svig.
18 Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
Mangens Snak er som Sværdhug, de vises Tunge læger.
19 Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
Sanddru Læbe bestaar for evigt, Løgnetunge et Øjeblik.
20 Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
De, som smeder ondt, har Svig i Hjertet; de, der stifter Fred, har Glæde.
21 Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
Den retfærdige times der intet ondt, gudløse oplever Vanheld paa Vanheld.
22 Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
Løgnelæber er HERREN en Gru, de ærlige har hans Velbehag.
23 Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
Den kloge dølger sin Kundskab, Taabers Hjerte udraaber Daarskab.
24 Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
De flittiges Haand skal raade, den lade tvinges til Hoveriarbejde.
25 Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
Hjertesorg bøjer til Jorden, et venligt Ord gør glad.
26 Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
Den retfærdige vælger sin Græsgang, gudløses Vej vildleder dem selv.
27 Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
Ladhed opskræmmer intet Vildt, men kosteligt Gods faar den flittige tildelt.
28 Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.
Paa Retfærds Sti er der Liv, til Døden fører den onde Vej.