< Miyambo 11 >

1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
Falsk vegt er fæl for Herren, men full vegt likar han godt.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
Kjem stormod, so kjem og skam, men smålåtne, dei hev visdom.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
Dei ærlege hev si uskyld til førar, men fals slær sin herre på hals.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Gods hjelper ikkje på vreidens dag, men rettferd frelser frå dauden.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
Ærleg manns rettferd jamnar hans veg, men den gudlause stuper ved gudløysa si.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
Ærlege folk ved si rettferd vert frelste, men dei falske vert fanga i eigen gir.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
Når ugudleg mann døyr, er det ute med voni; og vondskaps venting til inkjes vert.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
Rettferdig vert fria or trengsla, og ugudleg kjem i hans stad.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
Den skamlause tyner sin granne med munnen, men rettferdige friar seg ut med sin kunnskap.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
Gjeng det godt med rettferdige, fegnast byen, vert gudlause tynte, syng folk av gleda.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
Med velsigning frå ærlege folk kjem byen seg upp, men gudlause munn bryt han ned.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
Vitlaus er den som vanvyrdar sin granne, men vitug mann tegjer stilt.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
Den som fer med drøs, ber løynråd ut, men den hjarte-trugne løyner saki.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Der inkje styre er, lyt folket falla, men der dei rådvise er mange, der er frelsa.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
Borgar du for framand, er du ille faren, men han er trygg som hatar handtak.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
Ei yndefull kvinna vinn æra, og valdsmenner vinn seg rikdom.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
Ein godhjarta mann gjer vel mot si sjæl, men ein hardhjarta mann fer vondt med sitt eige kjøt.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
Den ugudlege vinn seg ei sviksam løn, men den som rettferd sår, fær varig løn.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
Stend du fast i rettferd, vinn du liv, men fer du etter vondt, då fær du daude.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
Dei range i hugen hev Herren ein stygg til, men han likar deim som ulastande ferdast.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Det kann du gjeva handi på, den vonde vert’kje urefst, men ætti åt rettferdige slepp undan.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
Som ein gullring i eit grisetryne er ei fager kvinna utan vit.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
Det rettferdige ynskjer, vert berre godt, det som gudlause vonar, vert til vreide.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
Ein strår ut og fær endå meir, ein annan vert arm av usømeleg sparing.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
Den som velsignar, skal trivast, og kveikjer du andre, vert sjølv du kveikt.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
Ein kornflår, honom bannar folket, men signing kjem yver den som sel korn.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
Den som strævar etter godt, han søkjer hugnad, men den som leitar etter vondt, han fær det yver seg.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
Den som lit på sin rikdom, han skal stupa, men rettferdige grønkar som lauv.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
Den som øydar sitt hus, skal erva vind, og narren vert træl åt den kloke.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
Rettferdig manns frukt er eit livsens tre, og sjæler vinn den vise.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Du ser rettferdig mann fær vederlag på jordi, kor mykje meir då den ugudlege og syndaren!

< Miyambo 11 >