< Miyambo 11 >

1 Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
Falsk vekt er en vederstyggelighet for Herren, men fullvektige lodder er ham til velbehag.
2 Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
Med overmot følger skam, men de ydmyke har visdom.
3 Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
De opriktiges rettsinn leder dem, men de troløses forvendte sinn ødelegger dem.
4 Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Gods hjelper ikke på vredens dag, men rettferdighet frir fra døden.
5 Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
Den ustraffeliges rettferdighet gjør hans vei jevn, men den ugudelige faller ved sin ugudelighet.
6 Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
De opriktiges rettferdighet frelser, men de troløse fanges i sin egen ondskap.
7 Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
Når et ugudelig menneske dør, blir hans håp til intet, og med det som de onde stunder efter, er det forbi.
8 Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
Den rettferdige utfries av trengsel, og den ugudelige kommer i hans sted.
9 Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
Med munnen ødelegger den gudløse sin næste, men ved sin kunnskap utfries de rettferdige.
10 Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
Når det går de rettferdige godt, jubler byen, og når de ugudelige omkommer, lyder fryderop.
11 Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
Ved de opriktiges velsignelse blir en by ophøiet, men de ugudeliges munn bryter den ned.
12 Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
Den som taler foraktelig om sin næste, er uten forstand; men en forstandig mann tier.
13 Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
Den som går omkring som baktaler, åpenbarer hemmeligheter; men den som er trofast i ånden, skjuler saken.
14 Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
Hvor det intet styre er, faller folket; men hvor det er mange rådgivere, der er frelse.
15 Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
Ille går det den som går i borgen for en fremmed; men den som skyr å gi håndslag, er sikker.
16 Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
En yndig kvinne vinner ære, og voldsmenn vinner rikdom.
17 Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
En godgjørende mann gjør vel mot sig selv, men en hårdhjertet mann ødelegger sig.
18 Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
Den ugudelige vinner en lønn som svikter, men den som sår rettferdighet, får en lønn som varer.
19 Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
Den som står fast i rettferdighet, ham blir det til liv; men den som jager efter ondt, volder sin egen død.
20 Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
En vederstyggelighet for Herren er de hvis hjerte er forvendt; men til velbehag for ham er de hvis vei er ustraffelig.
21 Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
Visselig, den onde blir ikke ustraffet, men de rettferdiges ætt slipper unda.
22 Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
Som en gullring i et svinetryne er en fager kvinne som er uten forstand.
23 Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
De rettferdiges attrå er bare det som godt er; de ugudelige har vrede i vente.
24 Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
Den ene strør ut og får ennu mere; den andre holder tilbake mere enn rett er, og det blir dog bare fattigdom.
25 Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
Den som velsigner, skal trives, og den som lesker andre, han blir selv lesket.
26 Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
Den som holder korn tilbake, ham banner folket; men velsignelse kommer over dens hode som selger korn.
27 Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
Den som søker hvad godt er, søker det som er til behag; men den som higer efter ondt, over ham kommer det onde.
28 Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
Den som setter sin lit til sin rikdom, han skal falle; men de rettferdige skal grønnes som løvet.
29 Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
Den som setter sitt hus i ulag, skal arve vind, og dåren blir en tjener for den vise.
30 Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
Den rettferdiges frukt er et livsens tre, og den vise fanger sjeler.
31 Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!
Se, den rettferdige får sin lønn på jorden, hvor meget mere da den ugudelige og synderen!

< Miyambo 11 >